Surah An-Nisa ( The Women )

Surah An-Nisa ( The Women ) - Chewa Aya count 176

E inu anthu! Opani Mbuye wanu yemwe adakulengani kuchokera mwa munthu mmodzi (Adam) ndipo adalenga mmenemo mkazi wake (Hawa), ndipo adafalitsa amuna ndi akazi ambiri kuchokera mwa awiriwo. Ndipo opani Allah yemwe kupyolera mwa Iye mumapemphana. Ndipo (sungani) chibale. Ndithudi Allah Ndimyang’aniri pa inu (akuona chilichonse chimene muchita).[105]
Ngati mwaopa kuti simungachite chilungamo pa amasiye (opaninso kusawachitira chilungamo akazi pamitala), choncho kwatirani amene mukuwafuna mwa akazi; awiri, kapena atatu, kapena anayi (basi). Koma ngati mukuopa kuti simungathe kuchita chilungamo, (kwatirani) mmodzi basi kapena amene manja anu akumanja adapeza (mdzakazi). Kutero kudzakuchititsani kuti musapendekere (kumbali yosalungama).[106]
Ndipo akazi apatseni chiwongo chawo monga mphatso. Koma (akazi anuwo) ngati atakupatsani mokoma mtima chilichonse (m’chiwongocho), idyani mokondwa ndi mothandizika nacho.[107]
Ozerezeka musawapatse chuma chanu chomwe Allah wachichita kukhala cholimbitsa matupi anu ndi moyo wanu. Koma adyetseni nacho ndikuwaveka nacho ndikuwauza mawu abwino (monga kuti: Mukadzakula ndikukhala olungama, tidzakupatsani chuma chanu).[108]
Ayeseni amasiye (akayandikira kukula nsinkhu kuti muone kuti atha kuchita ntchito yabwino ndi chuma chawo mukawapatsa), kufikira atafika nthawi yokwatira/kukwatiwa. Ndipo ngati mutawaona kuti ali ndi nzeru zabwino, apatseni chuma chawo. Musachidye mosasamala ndi mwachangu poopa kuti angakule. Ndipo amene ali opeza bwino adziletse (kulandira mphoto yolelera ana amasiyewo). Koma amene ali wosauka adye mwa ubwino (osati moononga). Ndipo pamene mukuwapatsa chuma chawo, funani mboni (zoonelera kuperekedwa kwa chumacho). Ndipo Allah ali Wokwana kukhala Muwelengeri (ndi Woyang’anira).[109]
Ndipo (wowasiirawo) aope (kusachita chilungamo), kuti naonso ngati atasiya ana awo ofooka pambuyo, akadawaopera (kuchenjeleredwa). Choncho aope Allah ndipo anene mawu olingana (kwa ana amasiyewo).
Allah akukulamulani za ana anu achimuna apate gawo lolingana ndi gawo la akazi awiri. Ngati akaziwo ali (opitilira) awiri, ndiye kuti adzalandira zigawo ziwiri mwa zigawo zitatu (2/3) za (chumacho) chimene wasiya (womwalira), ngati mwana wamkazi ndi mmodzi, apatsidwe gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2), naonso makolo ake awiri aliyense wa iwo alandile gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achuma chosiidwacho, ngati (womwalirayo) wasiya mwana (kapena mdzukulu). Koma ngati sadasiye mwana, ndipo makolo ake awiri ndiwo awasiira, ndiye kuti mayi wake alandire gawo limodzi mwamagawo atatu (1/3) achumacho, (ndipo bambo alandire 2/3). Ngati wakufayo wasiya abale, ndiye kuti mayi wake apeza gawo limodzi mwa magawo asanu ndi limodzi (1/6) achumacho. (Kugawa chumaku kuchitike) atachotsapo chimene iye adalamulira kuti adzachipereke kwakutikwakuti, kapena kulipira ngongole (zake). Atate anu ndi ana anu, simudziwa inu kuti ndani mwa iwo amene ali ndi chithandizo chapafupi kwa inu. Amenewa ndi malamulo omwe akhazikitsidwa ndi Allah. Ndithudi, Allah ngodziwa kwambiri, Ngwanzeru zakuya.[112]
Inunso mupata gawo limodzi mwa magawo awiri (1/2) achuma chimene akazi anu asiya ngati alibe mwana (kapena mdzukulu), ngati asiya mwana ndiye kuti inu mupata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) achuma chosiidwacho mutachotsapo zomwe adalamula kuti zipite kwakutikwakuti kapena ngongole zake, naonso akazi anu apata gawo limodzi m’magawo anayi (1/4) pa chuma chomwe mwasiya, ngati mulibe mwana (ndi mdzukulu). Koma ngati mwasiya mwana (ndi mdzukulu), (akaziwo) apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi atatu (1/8) pa chuma chomwe mwasiya mutachotsapo chomwe mudanena kuti chipite kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole (zanu). Ngati mwamuna kapena mkazi alowedwa m’malo pachuma pomwe alibe mwana (ndi mdzukulu) ngakhale makolo awiri, koma ali naye m’bale wake (wakuchikazi) kapena mlongo wake (wakuchikazinso) aliyense wa iwo apata gawo limodzi m’magawo asanu ndi limodzi (1/6). Ndipo ngati ali ochulukirapo, ndiye kuti agawirana gawo limodzi m’magawo atatu (1/3) a chumacho pambuyo pochotsapo chomwe chidanenedwa kuti chipita kwakutikwakuti kapena kulipira ngongole, popanda kupereka mavuto. Awa ndi malamulo ofunika omwe achokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri (pokhazikitsa malamulo); Woleza (pa akapolo Ake).[113]
Amenewo ndiwo malire a Allah; (musawalumphe). Ndipo amene angamvere Allah ndi Mtumiki Wake adzamulowetsa m’Minda yomwe pansi (ndi patsogolo pake) mitsinje ikuyenda. Adzakhala m’menemo nthawi yaitali. Kumeneko ndiko kupambana kwakukulu.
Koma amene anganyoze Allah ndi Mtumiki Wake, ndi kulumpha malire ake, (Allah) adzamulowetsa ku Moto; nadzakhala m’menemo nthawi yaitali. Ndipo adzapeza chilango chosambula.
Ndipo amuna awiri mwa inu amene akuchita zauve (monga kuchitana ukwati amuna okhaokha ‘matanyula’), akhaulitseni (powalanga). Tsono ngati atalapa ndikukonza bwino (mkhalidwe wawowo) asiyeni. Ndithudi, Allah Ngolandira kulapa, ndiponso Ngwachisoni chambiri.
Ndipo musakwatire akazi amene adakwatiwapo ndi atate anu, kupatula zomwe zidapita, (musabwerezenso kuzichita). Ndithudi, chinthu ichi nchauve ndipo nchodedwa ndiponso ndinjira yoipa.[117]
Kwaletsedwa kwa inu kukwatira amayi anu, ana anu, alongo anu, azakhali anu, amayi anu aang’ono kapena aakulu, ana achikazi am’bale wanu, ana achikazi a mlongo wanu, amayi anu amene adakuyamwitsani, alongo anu oberekedwa ndi amene adakuyamwitsanipo. Mayi a akazi anu, ana achikazi owapeza amene mukuwasunga woberekedwa ndi akazi anu omwe mwalowana nawo. Koma ngati simudalowane nawo, nkosaletsedwa kwa inu kukwatira ana awowo; ndi akazi a ana amuna omwe ngochokera kumisana yanu. Ndiponso nkoletsedwa kwa inu kukwatira mophatikiza mkazi ndi mchemwali wake obadwa naye, kupatula zomwe zidapita. Ndithudi Allah Ngokhululuka kwambiri Ngwachisoni zedi.
۞ Ndiponso (nkoletsedwa kwa inu kukwatira) akazi okwatiwa kupatula chimene manja anu akumanja apeza (mdzakazi). Ili ndi lamulo la Allah lomwe lili pa inu. Ndipo kwalolezedwa kwa inu (kukwatira akazi) omwe sali m’gulu ili. Afunefuneni ndi chuma chanu m’njira ya ukwati, osati chiwerewere. Choncho, amene mwawakwatira mwa iwo nkusangalala nawo, apatseni chiwongo chawo chomwe chakakamizidwa. Palibe kuipa kwa inu (kupereka) chomwe mwagwirizana m’malo mwa chomwe chidatchulidwa. Ndithudi, Allah Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya (pokhazikitsa malamulo Ake).
Ndipo amene sangathe mwa inu kupeza chuma chokwatilira mkazi amene ali mfulu wokhulupirira, (akwatireni adzakazi) achisungwana okhulupirira, mwa omwe manja anu akumanja apeza, Allah akudziwa kwambiri chikhulupiliro chanu. Ndinu amodzi kuchokera kwa wina ndi mnzake (nonsenu ndinu ana a Adam). Akwatireni ndi chilolezo cha mabwana awo, ndipo apatseni chiwongo chawo mwachilamulo. (Akwatireni) omwe ali akazi odzisunga, osati achiwerewere kapena ochita zibwenzi. Ndipo akakwatiwa, kenako nkuchita chauve, chilango chawo nditheka lachilango cha mfulu. Kumeneko (kukwatira akapoloko) ndilamulo kwa yemwe mwa inu akuopa kuti angachite chiwerewere. Koma ngati mutapirira (posiya kukwatira akapolo) ndibwino kwa inu kutero. Ndipo Allah Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.
Allah akufuna kukufotokozerani ndi kukutsogolerani kunjira za omwe adalipo patsogolo panu; ndiponso akufuna kulandira kulapa kwanu. Ndipo Allah Ngodziwa kwambiri, Ngwanzeru zakuya.
Allah akufuna kukupeputsirani, pakuti munthu adalengedwa wofooka (alibe mphamvu za thupi ngakhale zolimbana ndi zilakolako za moyo).
Ngati mudzitalikitsa kumachimo akuluakulu omwe mukuletsedwa, ndiye kuti tikufafanizirani zolakwa zanu (zing’onozing’ono) ndipo tidzakulowetsani malo aulemu.[119]
Amuna ndiayang’aniri pa akazi chifukwa choti Allah watukula ena pa ulemelero pamwamba pa ena, chifukwa cha chuma chawo chimene apereka. Choncho, akazi abwino ndi omwe ali omvera, odzisunga ngakhale amuna awo palibe pakuti Allah wawalamula kudzisunga. Ndipo akazi omwe mukuopa mnyozo wawo, achenjezeni; ndipo kenako achokereni pamphasa, (apo ayi), akwapuleni (kukwapula kosavulaza), koma ngati akukumverani, musawafunire njira yowavutitsira. Ndithu Allah ndi yemwe ali Wapamwamba, Wamkulu (kuposa inu nonse).[122]
Ndipo (inu aweruzi) ngati muopa mkangano pakati pawo (pa mwamuna ndi mkazi wake), tumizani nkhoswe ya kuchimuna ndi nkhoswe ya kuchikazi. Ngati iwo atafuna kuyanjanitsa, Allah awapatsa mphamvu zoyanjanitsira pakati pawo (okanganawo). Allah Ngodziwa nkhani zobisika, ndiponso Ngodziwa nkhani zoonekera.
Ndithudi, Allah sachitira (anthu) zosalungama ngakhale kanthu kolemera ngati kanyelere; ngati kanthuko kali kabwino amakachulukitsa ndi kupereka malipiro aakulu kuchokera kwa Iye.
Nanga zidzakhala bwanji tikadzabweretsa mboni pa m’badwo uliwonse ndikukubweretsa iwe (Mneneri Muhammad{s.a.w}) kuti ukhale mboni pa m’badwo uwu.
Tsiku limenelo aja omwe sadakhulupirire namunyoza Mtumiki, adzakhumba kuti nthaka ikadafafanizidwa pa iwo (akwiliridwe, asaukitsidwe). Ndipo sadzatha kum’bisira Allah nkhani iliyonse (m’zomwe adachita m’moyo wa pa dziko).
Kodi sukuwaona omwe adapatsidwa gawo la (nzeru zozindikira) buku (la Allah, omwe ndi Ayuda ndi Akhrisitu), akudzisankhira kusokera ndiponso akufuna mutasokera kusiya njira (yabwino).[125]
Mwa Ayuda alipo omwe amasintha mawu kuwachotsa m’malo mwake. Ndipo amanena (chabe ndi milomo yawo): “Tamva;” (pomwe mitima yawo ikunena): “Tanyoza.” (Ndipo akunena kuuza Mtumiki): “Imva koma wosamveredwa (ndipo pakati pakuyankhula kwawo amanena mawu akuti) ‘Raaina’ (ncholinga chomnenera kuti iye ndimbutuma), mokhotetsa malilime awo (mu zoyankhula zawo kuti akhale ngati akumunenera zabwino pomwe akumtembelera) ndi cholinga chotukwana chipembedzo (cha Chisilamu). Akadakhala kuti iwo adanena: “Tamva ndipo tamvera; ndipo imva, utiyang’anire,” (mmalo mwa kunena kwawo kwakuti: ‘Raaina’), zikadakhala zabwino ndizolingana kwa iwo. Koma Allah adawatembelera chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Sakhulupirira koma pang’ono basi.
Ndithudi Allah sangakukhululuke kuphatikizidwa (ndi chinachake), koma amakhululuka (machimo ena) osati amenewa kwa amene wamfuna. Ndipo amene angamphatikize Allah, ndithudi, wadzipekera uchimo waukulu.
Kodi sukuwaona omwe akudziyeretsa okha? Koma Allah amamuyeretsa amene wamufuna (pomulimbikitsa kuchita zabwino). Ndipo sadzaponderezedwa ngakhale ndi kachinthu kochepa konga kaulusi kokhala mkati mwakhokho la tende.[126]
Kodi ali ndi gawo la ufumu (wa Allah? Nchifukwa ninji akunyasidwa munthu wina akaninkhidwa utumiki)? Zikadatero ndiye kuti sakadawapatsa anthu ngakhale kochepa kwambiri monga khokho la tende.[128]
Choncho alipo ena mwa iwo amene anazikhulupirira izi, ndiponso alipo ena mwa iwo omwe adziika nazo kutali. Ndipo Jahannam ikukwanira kukhala Moto waukali wowatentha.
Kodi zingakhale bwanji litawabwerera vuto chifukwa cha zomwe manja awo adatsogoza? Kenako nkukudzera (iwe Mtumiki) uku akulumbira: “Tikulumbira Allah; sitinafune china chilichonse koma zabwino zokha ndi chimvano.”
Ndipo sitidamtumize mtumiki aliyense koma kuti azimveredwa mwa lamulo la Allah. Ngati akadakudzera pamene adadzichitira okha zoipa, (chifukwa chokafuna chiweruzo cha satana) napempha chikhululuko kwa Allah (naye) Mtumiki nkuwapempheranso chikhululuko, ndithudi, akadampeza Allah ali Wolandira kulapa kwawo ali Wachisoni chosatha.
Ndikulumbira (m’choonadi cha) Mbuye wako, iwo sangakhale okhulupirira moona pokhapokha akuyese muweruzi wawo pa zomwe akukangana pakati pawo. Kenako asaone vuto m’mitima yawo pa zomwe waweruza, ndipo adzipereke kwathunthu (pogonjera chiweruzo chako).[132]
Ndiponso tikadawatsogolera ku njira yoongoka (yokawafikitsa ku Munda wamtendere).
E inu amene mwakhulupirira! Khalani ochenjera (ndi adani anu; musanyengedwe nawo). Pitani (kunkhondo) gulu limodzilimodzi, kapena pitaniko nonsenu pamodzi (monga momwe Mtumiki angakulangizireni).
Ndipo ndithu alipo ena mwa inu otsalira m’mbuyo sapita ku nkhondo, (ndiponso amaletsa anzawo). Ngati vuto litakupezani, (yense wa iwo) amanena: “Allah wandichitira chisomo posakhala m’gulu lawo kumeneko.”
Koma ngati utakupezani ubwino wochokera kwa Allah (monga kupeza chuma chambiri chosiidwa ndi adani, kapena kupambana kumene) amanena ngati kuti padalibe chikondi pakati panu ndi pakati pake: “Kalanga ine! Ndikadakhala nawo pamodzi pa nkhondo imeneyi, (ndiye kuti) ndikadapambana; kupambana kwakukulu.”
Kodi sukuwaona omwe adauzidwa kuti: “Aletseni manja anu (kumenyana ndi osakhulupirira mpaka lidze lamulo lakumenyana)? Koma tsono pempherani Swala ndikupereka chopereka basi. Koma pamene adalamulidwa kumenyana, pompo gulu lina la iwo lidaopa anthu (osakhulupirira) ngati likuopa Allah kapena kuposerapo. Ndipo adati: “Mbuye Wathu! chifukwa ninji mwatilamula kumenyana? Ha! Mukadatichedwetsa kufikira nyengo yochepa, (zikadakhala bwino).” Nena: “Chisangalalo cha m’dziko n’chochepa. Koma tsiku lachimaliziro ndilabwino kwambiri kwa amene akuopa (Allah). Ndipo simudzaponderezedwa ngakhale pa chinthu chaching’ono monga ulusi wakhokho la tende!”
Chabwino chimene chakufikira (iwe munthu) ndiye kuti chachokera kwa Allah. Koma choipa chimene chakufikira ndiye kuti chachokera kwa iwe mwini (chifukwa cha zochita zako zoipa). Ndipo takutumiza (iwe Muhammad) kwa anthu kukhala Mtumiki. Ndipo Allah ndimboni yokwana.
Yemwe angamvere Mtumiki ndiye kuti wamvera Allah, (chifukwa chakuti zonse zomwe iye akulamula nzotumidwa ndi Allah). Ndipo amene atembenukire kutali (kunyoza iwe, ndiye kuti zoipa zili pa iye mwini). Sitidakutumize iweyo kukhala muyang’anili pa iwo.
Choncho menya nkhondo pa njira ya Allah, suukukakamizidwa (za anthu ena) koma iwe mwini, ndipo akhwirizire Asilamu. Ndithu Allah angatsekereze mtopola wa omwe sadakhulupirire. Ndipo Allah Ngwaukali kwambiri pomenya nkhondo ndiponso Wolanga kwabasi.
Ndipo pamene mwalonjeredwa; kulonjeredwa kwamtundu uliwonse (Salam) vomerani ndi malonje abwino oposa amenewo, kapena bwezani ofanana nawo. Ndithudi, Allah Ngowerengera chinthu chilichonse.
Kodi mwatani inu pokhala magulu awiri pa nkhani ya achiphamaso (achinyengo) pomwe Allah wawatembenuza chifukwa cha (zoipa) zomwe achita? Kodi mukufuna kuti mumuongole amene Allah wamlekelera kusokera? Ndipo amene Allah wamulekelera kusokera, simungathe kumpezera njira (yomuikira ku chilungamo).
Ndipo sikoyenera kwa wokhulupirira kupha wokhulupilila (mnzake mwadala) pokhapokha mwangozi. Ndipo yemwe wapha wokhulupilila mwangozi, apereke ufulu kwa kapolo wa Chisilamu ndi dipo lomwe alipereke kwa ofedwawo pokhapokha akakana okha (amulowa mmalo a womwalilayo), monga m’njira ya sadaka. Ngati wophedwayo ndi mnansi wa adani anu pomwe ali wokhulupilila, perekani ufulu kwa kapolo wa Chisilamu, (palibenso dipo lina). Ngati wophedwayo ndi mmodzi wa anthu omwe pakati panu ndi iwo pali chipangano (chosamenyana nkhondo), ndiye kuti amulowammalo ake apatsidwe dipo; apatsidwenso ufulu kapolo wa Chisilamu. Ndipo ngati sadapeze (zoterozo), asale miyezi iwiri yotsatana. Iyo ndiyo njira yolapira (pa uchimo wotere) yochokera kwa Allah. Ndipo Allah Ngodziwa Ngwanzeru zakuya.
E inu amene mwakhulupirira! Mukayenda pa njira ya Allah, musachite chinthu pokhapokha mutaonetsetsa bwino. Ndipo musanene kwa amene akukulonjerani Salamu (kuti): “Sindiwe wokhulupirira,” (nkumupha). Mukufuna zinthu zamdziko lapansi komatu kwa Allah kuli zopeza zambiri. Umo ndi momwe inunso mudalili kale; koma Allah adakuchitirani chifundo (choncho mudalowa m’Chisilamu. Penyetsetsani bwinobwino). Ndithu Allah Ngodziwa bwinobwino nkhani zonse zimene muchita.
Adzapata nyota zazikulu zochokera kwa Iye ndi chikhululuko ndi chisoni. Ndipo Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi.
Ndithudi amene angelo atenga miyoyo yawo, ali odzichitira okha zoipa (posasamuka ku Makka), adzawauza kuti: “Mudachitanji (pachipembedzo chanu?)” Iwo adzati: “Tidali ofooka ndi oponderezedwa padziko; (choncho sitidathe kuchita mapemphero athu).” (Angelo) adzati: “Kodi dziko la Allah silidali lotambasuka kotero kuti inu nkusamukira kwina m’menemo?” Iwowo malo awo ndi Jahannam. Taonani kuipa kwa malo obwerera.[136]
Ndipo amene angasamuke pa njira ya Allah (chifukwa cha chipembedzo chake,) apeza malo ambiri m’dzikomo othawira ndikupeza bwino. Ndipo amene angatuluke m’nyumba mwake kuti asamuke chifukwa cha Allah ndi Mtumiki Wake, kenako nkumpeza imfa (m’njira), ndithu malipiro ake atsimikizika kwa Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni chosatha.[137]
Ndipo ngati uli pamodzi (ndi Asilamu pankhondo) ndikuwatsogolera Swala, ndiye kuti gulu limodzi la iwo liimilire pamodzi ndi iwe ndikupemphera uku atagwirizira zida zawo. Ndipo akamaliza kulambira kwawo, apite kumbuyo kwanu (kuti akulondereni) ndipo lidze gulu lina lomwe silidapemphere, lipemphere nawe pamodzi; nawonso achenjere ndikugwirizira zida zawo (nkupemphera), chifukwa chakuti omwe sadakhulupirire akufuna kuti mutanyalanyaza zida zanu ndi katundu wanu angokuukirani nthawi imodzi. Koma sikulakwa kwa inu mutaika pansi zida zanu chifukwa chakuvutitsidwa ndi mvula kapena ngati mukudwala. Koma chenjeranaoni. Ndithudi Allah wawakonzera chilango choyalutsa osakhulupirira.[139]
Ndipo mpemphe chikhululuko Allah. Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni chosatha.
Ndipo amene angachite choipa (povutitsa ena), kapena kudzichitira yekha zoipa, kenako nkupempha chikhululuko kwa Allah, adzampeza Allah ali Wokhululuka kwabasi, Wachisoni chosatha. [144]
Ndipo amene angachite cholakwa (chaching’ono) kapena tchimo (lalikulu) kenako nkumponyera nalo yemwe sadalakwe (momunamizira), ndithudi wasenza bodza lamkunkhuniza ndi uchimo woonekera.[146]
Palibe ubwino m’zambiri zimene akunong’onezana kupatula amene akulamulira ena kupereka sadaka, kapena kuchita zabwino, kapenanso kuyanjanitsa pakati pa anthu (pakunong’onezana mawu). Amene angachite zimenezi, chifukwa chofuna chiyanjo cha Allah, tidzampatsa malipiro aakulu.
Ndithudi, Allah sakhululuka (uchimo) womphatikiza ndi chinthu china, (pochiyesa kuti ndi mnzake wa Allah). Koma Iye amakhululukira machimo ena omwe sali amenewo kwa yemwe wamfuna. Ndipo yemwe angamphatikize Allah (ndi milungu yabodza), ndithudi, wasokera kusokera konka nako kutali (ndi njira yachoonadi).
(Yemwe) Allah adamtembelera. Ndipo iye (satana) adati (kwa Allah): “Ndithudi, ndikadzipezera gawo lodziwika mwa akapolo anu.”[148]
(Satana) akuwalonjeza ndikuwapatsa chiyembekezo (pa zinthu zomwe sizingachitike). Ndithudi, satana sawalonjeza china koma chinyengo basi.
(Kulowa ku Munda wamtendere) sikuli pa kukhumba kwanu ngakhalenso pa kukhumba kwa anthu a buku (Ayuda ndi Akhrisitu). Amene angachite choipa, adzalipidwa (nacho), ndipo sadzapeza mtetezi ngakhale mpulumutsi kupatula Allah.
Ndipo amene angachite ntchito zabwino, mwamuna kapena mkazi, pomwe iye ali wokhulupirira, iwo ndiamene adzalowa ku Munda wamtendere. Ndipo sadzaponderezedwa pa chilichonse, ngakhale chochepetsetsa kwambiri ngati kamphako ka nthangala ya tende.
Kodi ndani yemwe ali ndi chipembedzo chabwino choposa yemwe walunjika nkhope yake kwa Allah, iye ali wochita zabwino ndipo akutsata njira ya Ibrahim woona pa chikhulupiliro. Ndipo Allah adasankha Ibrahim kukhala bwenzi.
Ndipo ngati mkazi ataona kwa mwamuna wake nkhanza ndi kumusala, palibe kulakwa pa iwo kuyanjana pakati pawo mwachimvano. Ndipo chimvano ndichabwino. (Munthu aliyense amaumilira chimene afuna) chifukwa chakuti mitima ya anthu imaumilira umbombo. Koma ngati muchita zabwino ndi kuopa Allah, ndithudi, Allah Ngodziwa nkhani zanu zonse zomwe muchita.
Ndipo inu simungathe kuchita chilungamo (chenicheni) pakati pa akazi ngakhale mutayesetsa chotani. Koma musapendekere (mbali imodzi); kupendekera kwathunthu kotero kuti nkumusiya (yemwe simukumfunayo) ngati kuti wapachikidwa (osadziwika kuti ngokwatiwa kapena ayi). Ndipo ngati mutayanjana ndi kuopa Allah (zingakhale bwino). Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi.
Koma ngati atalekana, Allah angalemeretse aliyense wa iwo kuchokera m’zabwino zake zochuluka ndipo Allah ali nazo zambiri, Ngwanzeru zakuya.
Amene afuna mphoto ya dziko lapansi, (afunefune kwa Allah). Kwa Allah ndikumene kuli mphoto ya pa dziko lapansi ndi ya tsiku lachimaliziro. Ndipo Allah Ngwakumva, Ngopenya.
E inu amene mwakhulupirira! Khalani oimiritsa chilungamo, opereka umboni chifukwa cha Allah; ngakhale kuti ubwere ndi masautso kwa inu, kapena kwa makolo anu, kapena kwa abale anu, ngakhale ali olemera kapena osauka, (musayang’ane zimenezo). Allah ndiye woyenera kuyang’ana za awiriwo. Choncho musatsate zilakolako ndi kusiya chilungamo. Ngati mukhotetsa (umboni), kapena kupewa (kupereka umboni) ndithudi nkhani zonse zomwe mukuchita Allah akuzidziwa.
(A chiphamaso) omwe akukuyembekezerani (kuti mavuto akugwereni), ngati mutapeza kupambana kochokera kwa Allah, amakuuzani: “Kodi sitidali nanu limodzi?” Koma ngati osakhulupirira atapeza gawo (lopambana), amanena (kwa osakhulupirira): “Kodi Sitidayandikire kukugonjetsani pamene tidali m’gulu lankhondo la okhulupirira koma timakutsekerezani kwa okhulupirira?” Koma Allah adzaweruza pakati panu tsiku la chiweruziro. Ndipo Allah sangawaikire njira osakhulupirira pa okhulupirira (kuti awagonjetse kotheratu).
Akungoyendayenda pakati pa awa ndi awa (pakati pa Asilamu ndi osakhulupirira). Iwo sali mbali iyi kapena mbali inayo. Ndipo amene Allah wamlekelera kuti asokere sungampezere njira yolungama.
Ngati mungaonetse chabwino, kapena kuchibisa, kapena kukhululukira zoipa, (zoterozo ndizo zofunika), ndithu Allah Ngokhululuka ndiponso Ngokhoza.
Anthu amene adapatsidwa buku (Ayuda) akukupempha (iwe Mtumiki) kuti uwatsitsire buku kuchokera kumwamba. Ndithudi, adampemphanso Mûsa zazikulu kuposa zimenezi pomwe adati: “Tiwonetse Allah poyera.” Choncho udawagwira moto wamphenzi chifukwa cha kuipitsa kwao (motowo udachotsa miyoyo yawo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo. Zitatero Allah adawapatsa moyo kachiwiri). Kenako iwo adapanga thole (mwana wang’ombe monga mulungu wawo) pambuyo powafikira chisonyezo choonekera. Koma tidawakhululukira zimenezo, ndipo tidampatsa Mûsa chisonyezo choonekera poyera.[153]
Ndipo tidatukula phiri la Al-Tur pamwamba pawo (Ayudawo) polandira pangano lawo; tidati kwa iwo: “Lowani pachipata (cha dziko ili la Sham) mutawerama.” Tidatinso kwa iwo: “Musalumphe malire pa nkhani ya Sabata.” Ndipo tidalandira kwa iwo pangano lokhwima.[154]
Choncho (tidawalanga) chifukwa chakuswa mapangano awo, ndi kukana kwawo zisonyezo za Allah, ndi kupha kwawo aneneri popanda choonadi, ndi kunena kwawo kwakuti: “Mitima yathu yakutidwa (siingathe kuzindikira zomwe ukunena iwe Muhammad {s.a.w}).” (Ai, Siinakutidwe ndi chilichonse), koma Allah waidinda zidindo chifukwa cha kusakhulupirira kwawo; tero sakhulupirira koma pang’ono pokha.
Chifukwanso cha kusakhulupirira kwawo ndi kumnamizira kwawo Mariya bodza lalikulu (kuti wabala Isa (Yesu) m’njira ya chiwerewere);
Ndikuyankhula kwawo (kwakuti): “Ife tamupha Mesiya Isa (Yesu) mwana wa Mariya, Mtumiki wa Allah; pomwe sadamuphe ndipo sadampachike pa mtanda. Koma adasokonezedwa (ndi munthu wina namuganizira kuti ndi Isa (Yesu). Ndithudi, amene akutsutsana pankhaniyi (Ayuda ndi Akhrisitu) ali m’chikaiko pa iyo; alibe kudziwa kotsimikizika, koma akungotsatira zongoganizira. Ndipo, sadamuphe mosimikiza (kuti ndi iye).
Palibe aliyense mwa anthu omwe adapatsidwa buku (Ayuda ndi Akhrisitu) koma kuti azamkhulupirira iye (Yesu kuti sadali mulungu) imfa yake (Yesuyo) isadadze (izi zizachitika pamene Yesuyo azabwerenso padziko lapansi kumapeto kwa dziko). Nayenso (Yesu) pa siku la chiweruziro adzaikira umboni pa iwo (kuti iye adali chabe kapolo wa Allah).
Chifukwa chakuchita kwawo zoipa, awo Ayuda, tidaletsa kwa iwo zinthu zabwino (zakudya) zomwe zidali zovomerezeka kwa iwo; ndiponso chifukwa cha kutsekereza kwawo anthu ambiri kuyenda panjira ya Allah.
Ndipo (tidavumbulutsanso chivumbulutso) kwa atumiki omwe takusimbira kale nkhani zawo komanso kwa atumiki ena omwe sitinakusimbire (nkhani zawo); ndipo Allah adayankhula ndi Mûsa mwachindunji.
(Iwo ndi) atumiki omwe adauza nkhani zabwino (kwa anthu abwino) ndi kuwachenjeza (oipa) kuti anthu asadzakhale ndi mtsutso pa Allah pambuyo pa (kudza kwa) atumikiwa. Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
E inu anthu a buku! Musamalumphe malire pa chipembedzo chanu. Ndipo musamamnenere Allah koma zowona (zokhazokha). Ndithu Mesiya Isa (Yesu) mwana wa Mariya, ndi mtumiki wa Allah (ndiponso ndi munthu wolengedwa) ndi liwu Lake lomwe adaliyika mwa Mariya ndiponso (ali) ndi mzimu (moyo) wochokera kwa Iye (Allah, monga mizimu ina yonse imachokera kwa Iye). Choncho Khulupirirani Allah ndi atumiki Ake. Musamanene: “Utatu wa Mulungu;” siyani, (zikhululupiliro za utatu wa Mulungu), kutero ndibwino kwa inu. Ndithudi, Allah ndi Mulungu m’modzi (basi). Ulemelero wake ngotukuka kutali ndi kukhala ndi mwana. Nzake zonse za kumwamba ndi pansi. Ndipo Allah ndiMtetezi Wokwanira.
Mesiya (Mneneri Isa {Yesu}) sangaone kunyozeka kukhala kapolo wa Allah, ngakhalenso angelo oyandikitsidwa (kwa Allah). Ndipo amene angaone kunyozeka pa ukapolo wake kwa Allah nadzitukumula, onse adzawasonkhanitsa kwa Iye (ndipo kenako nkuwalonga kung’anjo ya Moto).
Akukufunsa (iwe Mneneri, za malamulo a chuma cha munthu yemwe wafa osasiya mwana kapena kholo). Nena: “Allah akukulamulani pa zayemwe sadasiye mwana ndi kholo (kuti) ngati munthu atamwalira pomwe alibe mwana, koma ali ndi mlongo wake (wa bambo amodzi), choncho (mlongo wakeyo) alandire theka (½) la zomwe wasiya (womwalirayo). Nayenso angalandire chuma (chamlongo wake) ngati alibe mwana. Ndipo ngati iwo ali (alongo) awiri, ndiye kuti adzalandira magawo awiri mmagawo atatu (2/3) a zomwe wasiya. Ndipo ngati ali abale (angapo) amuna ndi akazi, ndiye kuti mwamuna aliyense alandire gawo lolingana ndi la akazi awiri. Umo ndi momwe Allah akukufotokozerani (malamulo Ake) mwatsatanetsatane kuti musasokere. Ndipo Allah Ngodziwa chilichonse.
Share