وَمَن يَعْمَلْ سُوٓءًا أَوْ يَظْلِمْ نَفْسَهُۥ ثُمَّ يَسْتَغْفِرِ ٱللَّهَ يَجِدِ ٱللَّهَ غَفُورًۭا رَّحِيمًۭا ﴿١١٠﴾
Ndipo amene angachite choipa (povutitsa ena), kapena kudzichitira yekha zoipa, kenako nkupempha chikhululuko kwa Allah, adzampeza Allah ali Wokhululuka kwabasi, Wachisoni chosatha. [144]