Surah An-Nisa ( The Women ) - Aya 94

Surah An-Nisa ( The Women ) - Chewa - Aya 94 Aya count 176

يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓا۟ إِذَا ضَرَبْتُمْ فِى سَبِيلِ ٱللَّهِ فَتَبَيَّنُوا۟ وَلَا تَقُولُوا۟ لِمَنْ أَلْقَىٰٓ إِلَيْكُمُ ٱلسَّلَٰمَ لَسْتَ مُؤْمِنًۭا تَبْتَغُونَ عَرَضَ ٱلْحَيَوٰةِ ٱلدُّنْيَا فَعِندَ ٱللَّهِ مَغَانِمُ كَثِيرَةٌۭ ۚ كَذَٰلِكَ كُنتُم مِّن قَبْلُ فَمَنَّ ٱللَّهُ عَلَيْكُمْ فَتَبَيَّنُوٓا۟ ۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِمَا تَعْمَلُونَ خَبِيرًۭا ﴿٩٤﴾
E inu amene mwakhulupirira! Mukayenda pa njira ya Allah, musachite chinthu pokhapokha mutaonetsetsa bwino. Ndipo musanene kwa amene akukulonjerani Salamu (kuti): “Sindiwe wokhulupirira,” (nkumupha). Mukufuna zinthu zamdziko lapansi komatu kwa Allah kuli zopeza zambiri. Umo ndi momwe inunso mudalili kale; koma Allah adakuchitirani chifundo (choncho mudalowa m’Chisilamu. Penyetsetsani bwinobwino). Ndithu Allah Ngodziwa bwinobwino nkhani zonse zimene muchita.
Share