وَلَن تَسْتَطِيعُوٓا۟ أَن تَعْدِلُوا۟ بَيْنَ ٱلنِّسَآءِ وَلَوْ حَرَصْتُمْ ۖ فَلَا تَمِيلُوا۟ كُلَّ ٱلْمَيْلِ فَتَذَرُوهَا كَٱلْمُعَلَّقَةِ ۚ وَإِن تُصْلِحُوا۟ وَتَتَّقُوا۟ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ غَفُورًۭا رَّحِيمًۭا ﴿١٢٩﴾
Ndipo inu simungathe kuchita chilungamo (chenicheni) pakati pa akazi ngakhale mutayesetsa chotani. Koma musapendekere (mbali imodzi); kupendekera kwathunthu kotero kuti nkumusiya (yemwe simukumfunayo) ngati kuti wapachikidwa (osadziwika kuti ngokwatiwa kapena ayi). Ndipo ngati mutayanjana ndi kuopa Allah (zingakhale bwino). Ndithudi, Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi.