Surah An-Nisa ( The Women ) - Aya 102

Surah An-Nisa ( The Women ) - Chewa - Aya 102 Aya count 176

وَإِذَا كُنتَ فِيهِمْ فَأَقَمْتَ لَهُمُ ٱلصَّلَوٰةَ فَلْتَقُمْ طَآئِفَةٌۭ مِّنْهُم مَّعَكَ وَلْيَأْخُذُوٓا۟ أَسْلِحَتَهُمْ فَإِذَا سَجَدُوا۟ فَلْيَكُونُوا۟ مِن وَرَآئِكُمْ وَلْتَأْتِ طَآئِفَةٌ أُخْرَىٰ لَمْ يُصَلُّوا۟ فَلْيُصَلُّوا۟ مَعَكَ وَلْيَأْخُذُوا۟ حِذْرَهُمْ وَأَسْلِحَتَهُمْ ۗ وَدَّ ٱلَّذِينَ كَفَرُوا۟ لَوْ تَغْفُلُونَ عَنْ أَسْلِحَتِكُمْ وَأَمْتِعَتِكُمْ فَيَمِيلُونَ عَلَيْكُم مَّيْلَةًۭ وَٰحِدَةًۭ ۚ وَلَا جُنَاحَ عَلَيْكُمْ إِن كَانَ بِكُمْ أَذًۭى مِّن مَّطَرٍ أَوْ كُنتُم مَّرْضَىٰٓ أَن تَضَعُوٓا۟ أَسْلِحَتَكُمْ ۖ وَخُذُوا۟ حِذْرَكُمْ ۗ إِنَّ ٱللَّهَ أَعَدَّ لِلْكَٰفِرِينَ عَذَابًۭا مُّهِينًۭا ﴿١٠٢﴾
Ndipo ngati uli pamodzi (ndi Asilamu pankhondo) ndikuwatsogolera Swala, ndiye kuti gulu limodzi la iwo liimilire pamodzi ndi iwe ndikupemphera uku atagwirizira zida zawo. Ndipo akamaliza kulambira kwawo, apite kumbuyo kwanu (kuti akulondereni) ndipo lidze gulu lina lomwe silidapemphere, lipemphere nawe pamodzi; nawonso achenjere ndikugwirizira zida zawo (nkupemphera), chifukwa chakuti omwe sadakhulupirire akufuna kuti mutanyalanyaza zida zanu ndi katundu wanu angokuukirani nthawi imodzi. Koma sikulakwa kwa inu mutaika pansi zida zanu chifukwa chakuvutitsidwa ndi mvula kapena ngati mukudwala. Koma chenjeranaoni. Ndithudi Allah wawakonzera chilango choyalutsa osakhulupirira.[139]
Share