Surah An-Nisa ( The Women ) - Aya 141

Surah An-Nisa ( The Women ) - Chewa - Aya 141 Aya count 176

ٱلَّذِينَ يَتَرَبَّصُونَ بِكُمْ فَإِن كَانَ لَكُمْ فَتْحٌۭ مِّنَ ٱللَّهِ قَالُوٓا۟ أَلَمْ نَكُن مَّعَكُمْ وَإِن كَانَ لِلْكَٰفِرِينَ نَصِيبٌۭ قَالُوٓا۟ أَلَمْ نَسْتَحْوِذْ عَلَيْكُمْ وَنَمْنَعْكُم مِّنَ ٱلْمُؤْمِنِينَ ۚ فَٱللَّهُ يَحْكُمُ بَيْنَكُمْ يَوْمَ ٱلْقِيَٰمَةِ ۗ وَلَن يَجْعَلَ ٱللَّهُ لِلْكَٰفِرِينَ عَلَى ٱلْمُؤْمِنِينَ سَبِيلًا ﴿١٤١﴾
(A chiphamaso) omwe akukuyembekezerani (kuti mavuto akugwereni), ngati mutapeza kupambana kochokera kwa Allah, amakuuzani: “Kodi sitidali nanu limodzi?” Koma ngati osakhulupirira atapeza gawo (lopambana), amanena (kwa osakhulupirira): “Kodi Sitidayandikire kukugonjetsani pamene tidali m’gulu lankhondo la okhulupirira koma timakutsekerezani kwa okhulupirira?” Koma Allah adzaweruza pakati panu tsiku la chiweruziro. Ndipo Allah sangawaikire njira osakhulupirira pa okhulupirira (kuti awagonjetse kotheratu).
Share