Select surah 1- Al-Fatihah ( The Opening ) 2- Al-Baqarah ( The Cow ) 3- Al-Imran ( The Famiy of Imran ) 4- An-Nisa ( The Women ) 5- Al-Maidah ( The Table spread with Food ) 6- Al-An'am ( The Cattle ) 7- Al-A'raf (The Heights ) 8- Al-Anfal ( The Spoils of War ) 9- At-Taubah ( The Repentance ) 10- Yunus ( Jonah ) 11- Hud 12- Yusuf (Joseph ) 13- Ar-Ra'd ( The Thunder ) 14- Ibrahim ( Abraham ) 15- Al-Hijr ( The Rocky Tract ) 16- An-Nahl ( The Bees ) 17- Al-Isra ( The Night Journey ) 18- Al-Kahf ( The Cave ) 19- Maryam ( Mary ) 20- Taha 21- Al-Anbiya ( The Prophets ) 22- Al-Hajj ( The Pilgrimage ) 23- Al-Mu'minoon ( The Believers ) 24- An-Noor ( The Light ) 25- Al-Furqan (The Criterion ) 26- Ash-Shuara ( The Poets ) 27- An-Naml (The Ants ) 28- Al-Qasas ( The Stories ) 29- Al-Ankaboot ( The Spider ) 30- Ar-Room ( The Romans ) 31- Luqman 32- As-Sajdah ( The Prostration ) 33- Al-Ahzab ( The Combined Forces ) 34- Saba ( Sheba ) 35- Fatir ( The Orignator ) 36- Ya-seen 37- As-Saaffat ( Those Ranges in Ranks ) 38- Sad ( The Letter Sad ) 39- Az-Zumar ( The Groups ) 40- Ghafir ( The Forgiver God ) 41- Fussilat ( Explained in Detail ) 42- Ash-Shura (Consultation ) 43- Az-Zukhruf ( The Gold Adornment ) 44- Ad-Dukhan ( The Smoke ) 45- Al-Jathiya ( Crouching ) 46- Al-Ahqaf ( The Curved Sand-hills ) 47- Muhammad 48- Al-Fath ( The Victory ) 49- Al-Hujurat ( The Dwellings ) 50- Qaf ( The Letter Qaf ) 51- Adh-Dhariyat ( The Wind that Scatter ) 52- At-Tur ( The Mount ) 53- An-Najm ( The Star ) 54- Al-Qamar ( The Moon ) 55- Ar-Rahman ( The Most Graciouse ) 56- Al-Waqi'ah ( The Event ) 57- Al-Hadid ( The Iron ) 58- Al-Mujadilah ( She That Disputeth ) 59- Al-Hashr ( The Gathering ) 60- Al-Mumtahanah ( The Woman to be examined ) 61- As-Saff ( The Row ) 62- Al-Jumu'ah ( Friday ) 63- Al-Munafiqoon ( The Hypocrites ) 64- At-Taghabun ( Mutual Loss & Gain ) 65- At-Talaq ( The Divorce ) 66- At-Tahrim ( The Prohibition ) 67- Al-Mulk ( Dominion ) 68- Al-Qalam ( The Pen ) 69- Al-Haaqqah ( The Inevitable ) 70- Al-Ma'arij (The Ways of Ascent ) 71- Nooh 72- Al-Jinn ( The Jinn ) 73- Al-Muzzammil (The One wrapped in Garments) 74- Al-Muddaththir ( The One Enveloped ) 75- Al-Qiyamah ( The Resurrection ) 76- Al-Insan ( Man ) 77- Al-Mursalat ( Those sent forth ) 78- An-Naba' ( The Great News ) 79- An-Nazi'at ( Those who Pull Out ) 80- Abasa ( He frowned ) 81- At-Takwir ( The Overthrowing ) 82- Al-Infitar ( The Cleaving ) 83- Al-Mutaffifin (Those Who Deal in Fraud) 84- Al-Inshiqaq (The Splitting Asunder) 85- Al-Burooj ( The Big Stars ) 86- At-Tariq ( The Night-Comer ) 87- Al-A'la ( The Most High ) 88- Al-Ghashiya ( The Overwhelming ) 89- Al-Fajr ( The Dawn ) 90- Al-Balad ( The City ) 91- Ash-Shams ( The Sun ) 92- Al-Layl ( The Night ) 93- Ad-Dhuha ( The Forenoon ) 94- As-Sharh ( The Opening Forth) 95- At-Tin ( The Fig ) 96- Al-'alaq ( The Clot ) 97- Al-Qadr ( The Night of Decree ) 98- Al-Bayyinah ( The Clear Evidence ) 99- Az-Zalzalah ( The Earthquake ) 100- Al-'adiyat ( Those That Run ) 101- Al-Qari'ah ( The Striking Hour ) 102- At-Takathur ( The piling Up ) 103- Al-Asr ( The Time ) 104- Al-Humazah ( The Slanderer ) 105- Al-Fil ( The Elephant ) 106- Quraish 107- Al-Ma'un ( Small Kindnesses ) 108- Al-Kauther ( A River in Paradise) 109- Al-Kafiroon ( The Disbelievers ) 110- An-Nasr ( The Help ) 111- Al-Masad ( The Palm Fibre ) 112- Al-Ikhlas ( Sincerity ) 113- Al-Falaq ( The Daybreak ) 114- An-Nas ( Mankind )
Translations English English - Yusuf Ali English - Transliteration English - Rowwad Translation Center English - Ahmed Ali English - Ahmed Raza Khan English - Arberry English - Daryabadi English - Hilali & Khan English - Talal Itani English - Maududi English - Mubarakpuri English - Pickthall English - Qarai English - Qaribullah & Darwish English - Sarwar English - Shakir English - Wahiduddin Khan Français Español Spanish Cortes Spanish Garcia Português Deutsch German Bubenheim & Elyas German Khoury German Zaidan Italiano Nederlands Dutch Leemhuis Dutch Siregar Русский Russian Абу Адель Russian Аль-Мунтахаб Russian Крачковский Russian Кулиев Russian Османов Russian Порохова Russian Саблуков Română Greek Svenska Shqip Shqip Feti Mehdiu Shqip Sherif Ahmeti Bosanski Bosnian Mlivo Български České České Nykl Norwegian Türkçe Turkish Alİ Bulaç Turkish Çeviriyazı Turkish Diyanet İşleri Turkish Diyanet Vakfı Turkish Edip Yüksel Turkish Elmalılı Hamdi Yazır Turkish Öztürk Turkish Suat Yıldırım Turkish Süleyman Ateş Polski Croatian Georgian Српски українська Macedonian Lithuanian Azəri Azerbaijani Məmmədəliyev & Bünyadov اردو Urdu Maududi Urdu Ahmed Raza Khan Urdu Jalandhry Urdu Qadri Urdu Jawadi Urdu Junagarhi Urdu Najafi 日本語 한국어 中文 Chinese (Traditional) Hindi Hindi Muhammad Farooq Khan മലയാളം Malayalam Karakunnu & Elayavoor தமிழ் Melayu Indonesian Indonesian Quraish Shihab Indonesian Tafsir Jalalayn বাংলা জহুরুল হক فارسى كوردی Pashto Тоҷикӣ Татарча ไทย ئۇيغۇرچە Ўзбек Uzbek Mikhailo Yakuboych ދިވެހި Sindhi অসমীয়া Bisayan Iranun Maguindanaon Dari Hebrew қазақ тілі Khmer Marathi Hausa soomaali Swahili Afar N'ko Akan Chewa Dagbani Kinyarwanda Lingala Luganda Luhya Malagasy Mõõré Yaw Amazigh Amharic
Your browser does not support the audio element. Ndikulumbira (angelo) amene amandanda m’mizere yondondozana, (popembedza ndi kugonjera Mbuye wawo).
Ndi omwe amalalika ulaliki (wa Allah ndi kumtamanda mochulukira).
Ndithu Mulungu wanu ndi mmodzi basi.
Mbuye wathambo ndi nthaka, ndi zapakati pake; ndiponso Mbuye wa kuvuma konse.
Ndithu tidalikongoletsa thambo lapafupi (ndi inu) ndi chokongoletsa cha nyenyezi (zowala).
Ndi kuti lisungidwe ku satana aliyense wogalukira (lamulo la Allah).
Kuti asamvere (zomwe zikunenedwa ndi) gulu lolemekezeka (la angelo). Ndipo akugendedwa (ndi kupirikitsidwa) mbali zonse.
Kuthamangitsidwa mwamphamvu; ndipo chilango chonkerankera patsogolo chili pa iwo.
Kupatula amene wazembetsa mawu (akumwamba), ndipo chikumtsatira iye chenje cha moto chowala kwambiri.
Tawafunsa (otsutsa zouka ku imfa): “Kodi iwo ngovuta kuwalenga kuposa zimene tidalenga, (monga: thambo, nthaka, nyenyezi ndi zina zotere)?” Ndithu Ife tidawalenga kuchokera ku dongo lonyata.
Koma iwe (Mneneri) ukudabwa (za kutsutsa kwawo kuuka ku imfa pomwe zisonyezo zilipo zambirimbiri), ndipo akukuchitira chipongwe (kudabwa kwako).
Ndipo akalalikiridwa, salalikirika.
Ndipo akachiona chisonyezo (chosonyeza kukhoza kwa Allah,) amachichitira chipongwe.
Ndipo osakhulupirira amanena: “Palibe chilipo apa, koma ndi matsenga woonekera poyera.”
“Kodi tikadzafa ndi kusanduka fumbi ndi mafupa, tidzatulutsidwanso (kuchokera m’manda tili amoyo)?”
“Pamodzi ndi makolo athu akale?”
Nena (iwe Mneneri): “Inde (mudzaukitsidwa inu pamodzi ndi makolo anu) uku inu muli onyozeka.”
Ndithu (kuukako) ndimkuwe umodzi adzangodzidzimuka ali moyo, akuyang’ana.
Ndipo adzanena (okanawo): “Kalanga ife! Kuonongeka nkwathu! Ili nditsiku lija lamalipiro!”
(Adzawauza): “Ili nditsiku la chiweruziro lomwe mumalitsutsa lija.”
(Kudzanenedwa kwa angelo): “Asonkhanitseni amene adali osalungama pamodzi ndi akazi awo (okana Allah) ndi milungu yawo imene amaipembedza,”
“Kusiya Allah, ndipo asonyezeni njira ya ku Jahannam.”
“Koma aimikeni pano chifukwa iwo afunsidwa (za chikhulupiliro chawo ndi zochita zawo):”
“Kodi nchifukwa ninji inu (opembedza mafano) simukupulumutsana (monga mumanenera pa dziko lapansi kuti mudzapulumutsana)?”
Koma iwo pa tsikulo adzagonjera ndi kudzipereka (ku lamulo la Allah).
Ndipo adzatembenukirana ndi kuyamba kufunsana (ndi kudzudzulana).
Ndipo (ofooka) adzanena (kwa odzikweza): “Inu mumatidzera kumbali komwe timakuganizira kuti nkwabwino (ndi kutichotsako kunka nafe ku njira yopotoka).
(Odzikweza) adzayankha: “Koma simudali okhulupirira.”
“Ndipo tidalibe nyonga zokuponderezerani inu, koma mudali anthu opyola malire (ndi kutuluka ku choonadi cha Allah).”
“Choncho mawu a Mbuye wathu (onena za chilango) atsimikizika pa ife; ndithu ife tichilawa (chilango).”
“Tidakusokeretsani; nafenso tidali osokera. (Choncho musatidzudzule).”
Ndithu iwo akathandizana chilango tsiku limenelo (la chiweruziro).
Ndithu (chilango chonga chimenecho) ndimomwe timawachitira olakwira (Allah).
Ndithu iwo ankati akauzidwa kuti palibe wopembedzedwa mwa choonadi koma Allah ankadzitukumula.
Ndipo ankanena: “Kodi ife tisiye kupembedza milungu yathu chifukwa cha zonena za mlakatuli, wopenga?”
Iyayi koma adawadzera ndi choonadi (Mthenga wawo Muhammad yemwe siwamisala kapena wolakatula zopeka) ndipo adawatsimikizira za atumiki.
Ndithu inu (osakhulupirira) mudzalawa chilango chowawa.
Ndipo simudzalipidwa kupatula zokhazo zimene mumachita.
Kupatula akapolo a Allah oyeretsedwa.
Kwa iwo kuli zopatsidwa zodziwika (ndi Mbuye wawo Allah),
Zipatso (zamtundu uliwonse); ndipo iwo adzalandira ulemu (waukulu),
Adzakhala pa makama (a mtengo wapatali) uku akuyang’anizana.
Uku zikuwazungulira zikho zodzazidwa ndi zakumwa zochokera m’kasupe woyenda nthawi zonse.
Woyera, wokoma kwa akumwa (zakumwazo).
(M’zakumwazo) mulibe zopweteketsa mutu (kwa ozimwa) ndiponso iwo sadzaledzera nazo.
Ndipo kwa iwo kudzakhala akazi oyang’ana iwo okha, ophanuka maso (okongola).
Onga ngati dzira (la nthiwatiwa) losungidwa (m’mapiko).
Ndipo adzayang’anizana ndi kuyamba kufunsana (pakati pawo.)
Adzanena wonena mmodzi wa iwo: “Ine ndidali ndi mnzanga (wopembedza mafano amene amatsutsana nane za chipembedzo ndi zophunzitsa za Qur’an yolemekezeka).”
Yemwe amandiuza: “Kodi iwe ndiwe mmodzi wa ovomereza?”
“Zakuti tikadzafa ndi kusanduka fumbi ndi mafupa, (tidzaukanso) ndi kulandira malipiro (pa zochita zathu)?”
(Wokhulupirira) adzanena (kwa anzake: “Inu anthu a kumtendere) kodi simungasuzumire (nane ku moto kuti timuone)?”
Choncho adzayang’ana ndipo adzamuona ali mkatikati mwa moto.
Adzanena: “Ndikulumbilira Allah! Udatsala pang’ono kuti undiononge (ndikadakuvomera paja pa dziko lapansi).”
“Ndipo pakadapanda chisomo cha Mbuye wanga, ndikadakhala mmodzi mwa opezeka ku Moto.”
“Kodi zili choncho kuti sitidzafanso (tizingosangalala m’Munda wamtendere).”
“Kupatula imfa yathu yoyamba ija, ndi kutinso ife sitilangidwa?”
Ndithu izi (zimene Allah waika m’Munda wamtendere) ndiko kupambana kwakukulu.
(Pofuna kupeza) zonga zimenezi ogwira ntchito agwire.
Kodi zimenezo ndilo phwando labwino kapena mtengo wa Zaqqum (wowawa kwambiri womwe anthu a ku Moto azikadya)?
Ndithu Ife taupanga (mtengo umenewu) kukhala mayeso ndi chilango cha anthu ochimwa (podzichitira okha chinyengo ndi kupembedza mafano.)
Umenewu ndimtengo omwe umatuluka pakatikati pa Jahannam (adaulenga kuchokera ku Moto).
Zipatso zake (nzoipa) ngati mitu ya asatana.
Ndithu iwo akadya mtengowo ndi kudzaza mimba zawo ndi zipatso zake (pakuti sakapeza chakudya china kupatula zipatso za mtengowo).
Kenako, ndithu kuwawa kwa mtengowo kosakanikirana ndi madzi owira kuzakhala pa iwo.
Kenako ndithu kobwerera kwawo ndi ku Jahannam.
Ndithu iwo adapeza makolo awo ali osokera.
Ndipo iwonso adatsata mapazi awo mothamanga.
Ndipo, ndithu akale ambiri adasokera patsogolo pawo.
Ndipo, ndithu tidatuma achenjezi kwa iwo.
Tapenya momwe adalili mapeto a omwe adachenjezedwa.
Kupatula akapolo a Allah, oyeretsedwa (iwo ndiwo anthu a ku Munda wamtendere).
Ndithu Nuh adatiitana, (ndipo tidamuyankha mayankho abwino), taonani kukhala bwino Ife Oyankha.
Ndipo tidampulumutsa iye ndi anthu ake ku vuto lalikulu.
Ndipo tidazichita zidzukulu zake kukhala zotsala (pa dziko, oipa ataonongeka).
Ndipo tidamsiira mbiri yabwino kwa mibadwo yodza pambuyo pake.
Mtendere ukhale pa Nuh pa zolengedwa zonse.
Ndithu umu ndimomwe Ife tilipirira ochita zabwino.
Ndithu iye ndi mmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
Ndipo ndithu m’gulu lake (la Nuh) muli Ibrahim.
Kumbuka pamene adadza kwa Mbuye wake ndi mtima wabwino (wogonjera malamulo).
Pomwe adanena kwa bambo wake ndi anthu ake: “Mukupembedza chiyani?”
“Ha! Milungu yopeka kusiya Allah, ndi imene mukuifuna?”
“Kodi maganizo anu ngotani pa Mbuye wa zolengedwa zonse?”
Ndipo adayang’ana nyenyezi mozama.
Ndipo adanena: “Ine ndine wodwala!”
Choncho iwo adatembenuka ndi kumsiya.
(Ibrahim) adapita mozemba ku mafano awo, ndipo adawauza (mwachipongwe:) “Bwanji simukudya (chakudya chomwe chaikidwa patsogolo panupo)?”
Atatero adawatembenukira ndi kuwamenya (mwamphamvu) ndi dzanja lamanja.
(Pamene adamva eni mafanowo) adadza kwa iye akuthamanga.
Anati: “Kodi mukupembedza (miyala) imene mwasema?”
“Chikhalirecho Allah ndiye adakulengani ndi zimene mukuchita!”
Iwo adati: “Mmangireni ng’anjo, ndipo mponyeni m’motowo.”
Adafuna kumchita chiwembu (kuti amuphe ndi moto), koma tidawachita kukhala onyozeka.
Ndipo (Ibrahim) adati: “Ndithu ine ndikupita kwa Mbuye wanga, Iye andiongolera.”
“E Mbuye wanga! Ndipatseni mwana yemwe adzakhale (mmodzi) mwa olungama!”
Ndipo tidamuuza nkhani yabwino ya mwana wofatsa, (mwanayo ndi Ismaila).
Ndipo (adabadwa ndi kuyamba kukula.) Pamene adakwana nsinkhu woyenda pamodzi ndi tate wake pochitachita za m’dziko (Ibrahim adayesedwa mayeso kupyolera m’maloto omwe adalota). Adati: “E mwana wanga! Ine kutulo ndikuona maloto (owona ochokera kwa Allah omwe akundilamula) kuti ndikuzinge (monga nsembe yopereka kwa Allah). Nanga ukuti bwanji?” (Mwana wabwino) adanena: “Bambo wanga! Kwaniritsani chimene mukulamulidwa. Ngati Allah afuna, mundipeza ndili mmodzi mwa opirira.”
Pamene adagonjera onse awiri (chofuna cha Allah), ndipo (Ibrahim) adam’goneka chakumphumi (ndipo adatsimikiza kumupha).
Ndipo tidamuitana: “E iwe Ibrahim!”
“Ndithu wavomereza maloto! (Choncho usamuphe mwana wakoyo).” Umo ndi momwe timawalipirira ochita zabwino.
Ndithu amenewa ndimayeso oonekera.
Ndipo tidampulumutsa pompatsa nyama yayikulu (yoti apereke nsembe).
Ndipo tidamsiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pake).
Mtendere ukhale pa Ibrahim!
M’menemo ndi mornwe timawalipirira ochita zabwino.
Ndithu iye adali mmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
Ndiponso tidamuuza nkhani yabwino (yoti akhala ndi mwana wotchedwa) Isihaqa; mneneri; wam’gulu la olungama.
Ndipo tidamdalitsa iye ndi (mwana wake) Isihaqa; ndipo m’mbumba ya awiriwa mudapezeka abwino ndi odzichitira zoipa owonekera.
Ndipo ndithu tidawachitira zabwino Mûsa ndi Haruna, (powapatsa uneneri ndi madalitso ambiri).
Ndipo tidawapulumutsa (awiriwa) ndi anthu awo ku vuto lalikulu.
Ndipo tidawathangata (powagonjetsera adani awo), ndipo iwo adali opambana.
Ndipo tidawapatsa (Mûsa ndi Haruna) buku losonyeza poyera (malamulo).
Ndipo tidawaongolera ku njira yolunjika.
Ndiponso tidawasiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pawo).
Mtendere ukhale pa Mûsa ndi Haruna!
Ndithu umu ndi momwe Ife timawalipirira ochita zabwino.
Ndithu awiriwa adali m’gulu la akapoio Athu okhulupirira.
Ndipo ndithu Iliyasa ndi mmodzi wa atumiki.
(Kumbuka) pamene adanena kwa anthu ake: “Bwanji simuopa (Allah)?”
“Mukupembedza (fano lotchedwa) Ba’la ndi kusiya (kupembedza) Wabwino zedi mwa olenga onse.”
“Allah, Mbuye wanu ndi Mbuye wa makolo anu akale?”
Koma adamtsutsa; ndithu iwo adzaonekera (ku Moto).
Kupatula akapolo a Allah amene ayeretsedwa (ndi Allah).
Ndipo tidamsiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pake).
Mtendere ukhale pa Iliyasiin!
Ndithu umo ndi mmene Ife timawalipirira ochita zabwino.
Ndithu iye ndimmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
Ndithu Luti ndi mmodzi wa atumiki.
(Kumbuka) pamene tidampulumutsa iye ndi anthu ake onse.
Kupatula nkhalamba yachikazi; idali mwa otsalira.
Kenako tidawaononga enawo (omwe adali oipa).
Ndithu inu (a mumzinda wa Makka) mumadutsa pa malo pawopo m’mawa,
Ndi usiku. Kodi bwanji simuzindikira?
Ndithu Yunusu ndi mmodzi wa atumiki.
(Kumbuka) pamene adathawira m’chombo chodzazidwa (ndi katundu).
Choncho adachita mayere, ndipo adali m’gulu la omgwera (mayerewo).
Choncho nsomba idammeza uku ali wodzudzulidwa.
Kukadapanda kuti iye adali m’modzi mwa otamanda ndi kulemekeza Allah).
Akadakhala m’mimba mwake mpaka tsiku loukitsidwa (zolengedwa ku imfa).
Koma tidamponya pa gombe uku ali wodwala.
Ndipo tidammeretsera mmera wa mtundu wa nkhaka.
Ndipo (atachira) tidamtuma ku anthu okwana zikwi zana limodzi (100,000) kapena kupambana apa.
Ndipo adakhulupirira (ndi kuvomereza ulaliki wake); choncho tidawapatsa chisangalalo kufikira nthawi (ya imfa yawo).
Choncho afunse: “Kodi Mbuye wako ndiye woyenera ana aakazi, ndipo iwo aamuna? (Pomwe iwo akabereka mwana wamkazi amanyansidwa naye)!”
Kapena kuti tidalenga angelo kukhala akazi, iwo akuona?
Chenjera ndi bodza lawolo, ndithu iwo akunena:
“Allah wabereka.” Ndithu iwo ndi abodza.
Kodi Iye adasankha ana aakazi kusiya aamuna?
Kodi nchiyani chakupezani (kuti muweruze mopanda chilungamo); nanga mukuweruza bwanji (zimenezi)?
Kodi bwanji simukumbukira, (mwaiwala zisonyezo Zake zodabwitsa ndi kupatukana kwake ndi zimenezo)?
Kapena inu muli ndi umboni woonekera (wochokera kumwamba)?
Tabweretsani buku lanulo (momwe mwalembedwa zimenezi) ngati mukunena zoona.
Ndipo adapeka chibale pakati pa Iye (Allah) ndi ziwanda; (pomwe ziwanda nzobisika kwa iwo). Ndithu ziwanda zimadziwa kuti iwo osakhulupirira akaonekera (kwa Allah kuti aweruzidwe)!
Walemekezeka Allah! Ndi kupatukana ndi zimene akumnamizira!
Koma akapolo a Allah oyeretsedwa (ali kutali ndi zimene akusimba osakhulupirirazi).
Ndithu inu (osakhulupirira) ndi zimene mukuzipembedza (kusiya Allah),
Ndi zimenezo simungamsokeretse aliyense.
Kupatula yemwe (Allah adadziwa kuti) ngolowa ku Jahannam.
Ndipo (angelo adanena): “Aliyense mwa ife ali ndi malo ake odziwika.”
“Ndipo ndithu (ena mwa) ife ngondanda m’mizere (ya mapemphero nthawi zonse).”
“Ndipo (ena mwa) ife ngolemekeza (Allah nthawi zonse ndi kumtamanda ndi kumpatula ku zinthu zosayenerana ndi ulemelero wake).”
Ndipo (osakhulupirira) ankati:
“Tikadakhala ndi buku monga lomwe anthu akale adali nalo.”
“Tikadakhala akapolo a Allah, oyeretsedwa.”
Koma (pamene lidawadzera bukulo), adalikana; choncho posachedwa adziwa (zotsatira zake).
Ndipo ndithu liwu lathu lidatsogola kwa akapolo athu otumidwa.
(Kuti) ndithu iwo ngopulumutsidwa.
Ndipo ndithu asilikali Athu ndi opambana.
Choncho, asiye kwa kanthawi kochepa.
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona!
Kodi chilango chathu akuchifulumizitsa?
Choncho chikadzatsika pabwalo lawo, udzakhala mmawa woipa kwa ochenjezedwa!
Ndipo asiye kwa kanthawi kochepa.
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona.
Mbuye wako, Mwini ulemelero, wapatukana ndi zimene akumnamizira (osakhulupirira).
Ndipo mtendere ukhale pa atumiki onse.
Ndipo kuyamikidwa konse nkwa Allah, Mbuye wa zolengedwa zonse.