Surah Fatir ( The Orignator )

Surah Fatir ( The Orignator ) - Chewa Aya count 45

Kuyamikidwa konse nkwa Allah (Yekha) Muumbi wa thambo ndi nthaka (popanda chofanizira), amene adachita angelo kukhala atumwi eni mapiko, awiriawiri; atatuatatu; ndi anayianayi. Amaonjezera mkulenga monga momwe afunira, (palibe chimene chingakanike kwa Iye). Ndithu Allah Ngokhoza chilichonse.[338]
Chifundo chimene Allah angatsekule kwa anthu, palibe amene angachitsekereze. Ndipo chimene angachiletse palibe amene angachipereke kupatula Iye. Ndipo Iye ndi Mwini mphamvu zoposa, Wanzeru zakuya.
E inu anthu! Kumbukirani chisomo cha Allah chomwe chili pa inu (pomthokoza). Kodi alipo Mlengi wina osati Allah amene angakupatseni rizq kuchokera kumwamba ndi pansi? Palibe wina wopembedzedwa mwachoonadi, koma Iye. Nanga mukutembenuzidwira kuti?
Ndipo ngati angakutsutse ndithu adatsutsidwanso atumiki amene adalipo patsogolo pako. Ndipo zinthu zonse zidzabwezedwa kwa Allah.
Amene sadakhulupirire (Allah ndi Mtumiki Wake), pa iwo padzakhala chilango chaukali; koma amene akhulupirira ndi kumachita zabwino, iwo adzapeza chikhululuko ndi malipiro aakulu.
Kodi amene zochita zake zoipa zakometsedwa kwa iye nkumaziona kuti nzabwino, (ngolingana ndi amene waongoka ndi chiongoko cha Allah kotero kuti chabwino nkuchiyesa chabwino; choipa nkuchiyesa choipa?) Ndithu Allah akumlekelera kuti asokere yemwe wamfuna (chifukwa chakuti safuna kuongoka), ndipo akuongola amene wam’funa. Choncho moyo wako usaonongeke chifukwa chowadandaula iwo. Ndithu Allah Ngodziwa zonse zimene (iwo) akuchita.
Ndipo Allah ndiamene amatumiza mphepo; choncho imagwedeza mitambo (ya mvula) ndipo timaifikitsa ku dziko lakufa. Ndipo kupyolera m’madzi otuluka mmitamboyo; timaiwukitsa nthaka pambuyo pakufa kwake, momwemonso ndimmene kudzakhalira kutuluka akufa (m’manda tsiku la chiweruziro).
Ndipo Allah adakulengani ndi dothi; kenako ndi dontho la umuna; kenako adakupangani amuna ndi akazi. Ndipo mkazi aliyense satenga mimba ndiponso sabala koma kupyolera m’kudziwa Kwake (Allah). Ndipo amene wapatsidwa moyo, sapatsidwa moyo wautali ndiponso sachepetsedwa moyo wake, koma zonsezo zili m’buku (la Allah). Ndithu zimenezo kwa Allah nzosavuta.
Ndipo nyanja ziwiri (ya madzi ozizira ndi yamadzi amchere) sizili zofanana, iyi yamadzi okoma, ozuna, ndi omweka bwino kamwedwe kake; ndi iyi (ya madzi) amchere owawa. Ndipo kuchokera m’zonsezi, mumadya nyama yamatumbi (nsomba zaziwisi). Ndipo mumatulutsa zodzikongoletsera (zimene) mumazivala; ndipo m’menemo ukuona zombo zikung’amba madzi kuti mufunefune ubwino Wake (wa Allah) ndi kutinso inu muthokoze.
Ngati mutawapempha (mafanowo), sangamve kuitana kwanu, ndipo ngati atamva sangakuyankheni (chifukwa alibe kukhoza kulikonse). Ndipo pa tsiku lomalizira, adzakana kuphatikiza kwanu. Ndipo palibe (aliyense) angakuuze monga momwe akukuuzira (Allah) Wodziwa kwambiri.
E inu anthu! Inu ndiosaukira (chinthu chilichonse) kwa Allah; koma Allah Ngwachikwanekwane (sasaukira chilichonse kwa inu); Wotamandidwa (ndi zolengedwa zonse).
Ndipo wosenza, sadzasenza mtolo wa wina. (Aliyense adzasenza mtolo wa machimo ake). Ngakhale amene walemedwa ndi mtolo wake ataitana (wina) chifukwa cha mtolo wake kuti amsenzere silidzatengedwa ngakhale gawo pang’ono la mtolowo (ndi munthu ameneyo), ngakhale atakhala m’bale wake. Ndithu ukuchenjeza okhawo amene akuopa Mbuye wawo pomwe sakumuona, ndipo akupemphera Swala moyenera, ndipo yemwe akudziyeretsa, ndithu akudziyeretsa yekha, (ubwino wake umubwerera iye mwini); ndipo mabwelero (a zolengedwa zonse) ndi kwa Allah (basi).
Ndipo wakhungu ndi wopenya ngosafanana, (woyenda pa njira ya choona ndi wosokera ngosafanana).
Ndipo amoyo ndi akufa safanana (amene mitima yawo ili ndi moyo pokhala ndi chikhulupiliro, ndi amene mitima yawo ili yakufa posakhala ndi chikhulupiliro, ngosafanana). Ndithu Allah akumumveretsa amene wam’funa; koma iwe sungathe kumumveretsa amene ali m’manda.
Iwe sindiwe chinthu china, koma ndiwe mchenjezi.
Ndithu Ife takutuma mwachoona kuti unene nkhani yabwino (yokalowa ku Munda wamtendere kwa amene akhulupirira), ndi kuti uchenjeze (za chilango cha Moto kwa amene sadakhulupirire). Ndipo palibe m’badwo uliwonse koma mchenjezi adapitamo.
Ndipo ngati angakutsutse (sichachilendo), ndithu amene adali patsogolo pawo adatsutsanso. Aneneri awo adawadzera ndi zizindikiro zoonekera poyera, ndi malemba ndi buku lounikira (njira yabwino).
Kenako ndidawalanga (ndidawaononga) amene adatsutsa. Nanga chidali bwanji chilango Changa (pa iwo).
Kodi sudaone kuti Allah amatsitsa madzi kuchokera ku mitambo? Choncho kupyolera m’madziwo tatulutsa zipatso zautoto wosiyanasiyana (zakuda, zofiira, zachikasu, zobiriwira, pomwe madzi ake ndiamodzi omwewo). Ndipo m’mapiri muli timizere; toyera ndi tofiira tosiyana utoto wake, ndi (tina) takuda kwambiri.
Kuti akawakwaniritsire malipiro awo ndi kuwaonjezera zabwino Zake; ndithu Iye Ngokhululuka kwabasi; Ngothokoza kwambiri.
Ndipo adzanena (pakuthokoza kwawo): “Kutamandidwa konse nkwa Allah Amene watichotsera madandaulo; ndithu Mbuye wathu Ngokhululuka kwambiri, Ngothokoza kwabasi.”
Koma amene sadakhulupirire, wawo ndi moto wa Jahannam sikudzaweruzidwa kwa iwo kuti afe, ngakhale chilango chake sichidzachepetsedwa pa iwo. Umo ndimmene tikumlipirira aliyense wokanira (mtendere wa Allah).
Ndipo m’menemo iwo adzakuwa (adzalira uku akunena): “Mbuye wathu! Titulutseni (m’Moto ndi kutibweza pa dziko lapansi); tikachita ntchito zabwino, osati zija tinkachita.” (Allah adzawauza): “Kodi sitidakupatseni moyo wokwanira wotheka kukumbuka kwa wokumbuka? Ndiponso mchenjezi adakudzerani. Choncho lawani (chilango). Ndipo anthu ochita zoipa alibe mpulumutsi.”
Iye ndi Yemwe wakuchitani kukhala osiyirana pa dziko lapansi (akufa ena, ena nkulowa m’malo mwawo). Ndipo amene sadakhulupirire, kuipa kwa kusakhulupirirako kuli kwa iye mwini. Ndipo kusakhulupirira kwa osakhulupirira sikuwaonjezera chilichonse kwa Mbuye wawo, koma mkwiyo basi. Ndiponso kusakhulupirira kwa osakhulupirira sikuwaonjezera chilichonse, koma kutayika basi.
Nena: “Kodi mwawaona aphatikizi anu (awa) amene mukuwapembedza m’malo mwa Allah? Tandionetsani, ndimbali iti ya nthaka adalenga; kapena iwo ali ndi gawo m’thambo; (gawo lakulenga thambo?) Kapena tidawapatsa buku (Qur’an iyi isadadze) kotero kuti ali ndi umboni wapoyera wochokera m’menemo (wotsimikizira chipembedzo chawo chamafano)? Koma ochita zoipa salonjezana ena kwa ena china chake koma zachinyengo basi.
Ndipo (awa osakhulupirira, kale) adalumbilira Allah, kulumbira kwawo kwakukulu, kuti ngati adzawadzera mchenjezi, adzakhala oongoka kuposa mbadwo uliwonse. Koma pamene mchenjezi adawadzera, palibe chilichonse chidaonjezeka kwa iwo, koma kukana (choonadicho).
Chifukwa cha kudzikweza pa dziko ndi kuchita chiwembu choipa. Ndipo chiwembu choipa sichingamuzinge aliyense koma mwini (yemwe) wachitayo. Kodi akuyembekeza china chosakhala machitidwe (a Allah) amene adawapititsa pa anthu akale. Koma supeza kusintha pa machitidwe a Allah. Ndipo supeza kutembenuka pa machitidwe a Allah.
Share