Surah Fatir ( The Orignator ) - Aya 37

Surah Fatir ( The Orignator ) - Chewa - Aya 37 Aya count 45

وَهُمْ يَصْطَرِخُونَ فِيهَا رَبَّنَآ أَخْرِجْنَا نَعْمَلْ صَٰلِحًا غَيْرَ ٱلَّذِى كُنَّا نَعْمَلُ ۚ أَوَلَمْ نُعَمِّرْكُم مَّا يَتَذَكَّرُ فِيهِ مَن تَذَكَّرَ وَجَآءَكُمُ ٱلنَّذِيرُ ۖ فَذُوقُوا۟ فَمَا لِلظَّٰلِمِينَ مِن نَّصِيرٍ ﴿٣٧﴾
Ndipo m’menemo iwo adzakuwa (adzalira uku akunena): “Mbuye wathu! Titulutseni (m’Moto ndi kutibweza pa dziko lapansi); tikachita ntchito zabwino, osati zija tinkachita.” (Allah adzawauza): “Kodi sitidakupatseni moyo wokwanira wotheka kukumbuka kwa wokumbuka? Ndiponso mchenjezi adakudzerani. Choncho lawani (chilango). Ndipo anthu ochita zoipa alibe mpulumutsi.”
Share