وَلَوْ يُؤَاخِذُ ٱللَّهُ ٱلنَّاسَ بِمَا كَسَبُوا۟ مَا تَرَكَ عَلَىٰ ظَهْرِهَا مِن دَآبَّةٍۢ وَلَٰكِن يُؤَخِّرُهُمْ إِلَىٰٓ أَجَلٍۢ مُّسَمًّۭى ۖ فَإِذَا جَآءَ أَجَلُهُمْ فَإِنَّ ٱللَّهَ كَانَ بِعِبَادِهِۦ بَصِيرًۢا ﴿٤٥﴾
Ndipo Allah akadamalanga anthu chifukwa cha zomwe alakwa, sakadasiya pamwamba pake (pa nthaka) chamoyo chilichonse; koma Iye amawalekelera mpaka nthawi yomwe adaiikayo. Choncho nthawi yawo ikadzawadzera, (pompo adzalangidwa). Ndithu Allah akuwadziwa bwino akapolo Ake.