Surah Al-Anfal ( The Spoils of War )

Surah Al-Anfal ( The Spoils of War ) - Chewa Aya count 75

Akukufunsa za chuma cholandidwa pa nkhondo (mmene chingagawidwire). Nena: “Chuma cholanda pa nkhondo ndi cha Allah ndi Mtumiki (ndiamene ali olamula kagawidwe kake); choncho, muopeni Allah ndipo yanjanani mwachibale pakati panu. Mverani Allah ndi Mtumiki Wake, ngati mulidi okhulupirira.”[189]
Ndithu okhulupirira, enieni ndi amene akuti Allah akatchulidwa mitima yawo imadzadzidwa ndi mantha; pamenenso Ayah Zake zikuwerengedwa kwa iwo zimawaonjezera chikhulupiliro, ndipo amayadzamira kwa Mbuye wawo Yekha basi; (sakhulupirira nyanga ndi mizimu ya anthu akufa).[190]
Amene amaimilira kupemphera napereka chimene tawapatsa, (pa njira ya Allah, ndikuthandiza ovutika).
Awa (okhala ndi makhalidwe otere) ndi amene ali okhulupirira mwachoonadi. Iwo adzapeza ulemelero (wapamwamba) kwa Mbuye wawo, ndi chikhululuko ndi zopatsidwa zaulemu.
Monga mmene Mbuye wako adakulamulira kutuluka m’nyumba yako (kupita ku Badr kukachita nkhondo ndi osakhulupirira) mwachoonadi, ndithu gulu lina la okhulipirira silidafune (kuchoka kukakumana ndi adani).[191]
Akutsutsana nawe (pa chinthu) choona pambuyo pakuti chaonekera poyera. (Kukuwaipira kukumana ndi adani) ngati kuti akubusidwa kunka ku imfa akuona.
(Kumbukirani, E inu okhulupirira!) Pamene Allah anakulonjezani gulu limodzi mwa magulu awiri kuti likhale lanu (kuti mumenyane nalo). Koma inu mukufuna lopanda mphamvu kuti likhale lanu (kuti ndilo mumenyane nalo). Koma Allah akufuna kuchitsimikiza choonadi ndi mawu Ake ndi kudula mizu ya osakhulupirira, (pomenyana ndi gulu lamphamvulo, omwe ndi ankhondo a Chikuraishi).
(Kumbukirani) pamene mudali kupempha Mbuye wanu chithandizo, ndipo anakuyankhani kuti: “Ndithudi, Ine ndikuthandizani ndi chikwi cha angelo otsatizana potsika, (omenya nkhondo).”
Ndipo Allah sadachite ichi koma kuti chikhale nkhani yabwino (yosangalatsa), ndi kuti mitima yanu ikhazikike ndi chimenecho. Ndipo palibe chipulumutso (chothandiza) koma chimene chachokera kwa Allah. Ndithu Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.[192]
(Kumbukirani) pamene anakugonetsani tulo tomwe tidali mtendere wochokera kwa Iye, ndipo anavumbwitsa mvula pa inu yochokera ku mitambo kuti akuyeretseni nayo (matupi anu) ndikukuchotserani manong’onong’o a satana, ndi kuipatsa mphamvu mitima yanu ndiponso ndi kulimbikitsa mapazi anu (pamchenga).
(Kumbukira) pamene Mbuye wako anawauza angelo kuti: “Ine ndili pamodzi nanu (pokulimbikitsani ndi chithandizo Changa). Alimbikitseni amene akhulupirira, ndipo ndidzathira mantha mmitima mwa amene sadakhulupirire. Choncho amenyeni mmwamba mwa makosi awo, ndi kuwadula nsonga za zala zawo (zimene akugwilira zida).
Izi ndi chifukwa chakuti iwo anatsutsana ndi Allah ndi Mtumiki wake (iwo podziika mbali ina kusiya komwe kudali Allah). Amene anatsutsana ndi Allah ndi Mtumiki Wake, ndithu Allah ndi wolanga kwambiri (amalanga ndi chilango choopsa).
Chimenecho ndi chilango (cha Allah E inu Maquraish)! Choncho chilaweni. Ndithu osakhulupirira adzapeza chilango cha Moto.
Ndipo amene adzawatembenuzire msana kuthawa pa tsikulo - osati kutembenuka (kwa ndale) kofuna kumenyana kapena kukalowa m’gulu (la Asilamu ena) - ndiye kuti adziitanira mkwiyo wochokera kwa Allah; ndipo malo ake ndi ku Jahannam, kumeneko ndi ku malo koipa kubwererapo.
Inu simudawaphe (ndi mphamvu zanu) koma Allah ndi Yemwe anawapha; siudawagende pamene udagenda koma Allah ndi amene anawagenda (pofikitsa mchenga m’maso mwawo, wachita zimenezi) kuti awachitire zabwino Asilamu powapatsa dalitso labwino lochokera kwa Iye. Ndithu Allah Ngwakumva, Ngodziwa.[193]
Izi akuchitirani (pakalipano), ndithudi Allah afooketsa ndale za osakhulupirira.
Ngati mwakhala mukufuna chiweruzo (pogwilira nsalu yovindikira Ka’aba kuti mupambane pa nkhondo), chiweruzo chakudzerani (chokomera Asilamu). Ndipo ngati musiya (kuwazunza okhulupirira kapena kusiya kunyoza Allah) chikhala chinthu chabwino kwa inu. Koma ngati mubwereza (kuwaputa) nafenso tidzabwereza (kukulangani). Gulu lanu lankhondo silikuthandizani kanthu ngakhale lichuluke chotani. Ndipo Allah ali pamodzi ndi okhulupirira.
Ndipo musakhale monga aja achinyengo omwe akunena: “Tamva (choonadi ndipo tachisunga),” pomwe iwo sakumva (kumva kochigonjera).
Ndithu nyama zoipitsitsa pamaso pa Allah ndi agonthi, abubu amene alibe nzeru, (omwe ndi aphatikizi ndi anthu achinyengo).
Ndipo Allah akadadziwa mwa iwo (ndi kudziwa kwake kopanda chiyambi); kuti muli ubwino (pakuwamveretsa Qur’an ndi kuwazindikiritsa) akadawamveretsa. (Koma chikhalidwe chawo chili cha mtundu umenewo) ndipo ngakhale akadawamveretsa (Qur’an ndikuwazindikiritsa) akadatembenuka m’mbuyo uku akunyoza (chifukwa cha kugonjera zilakolako zawo).
E inu amene mwakhulupirira muvomereni Allah (pa zimene akukulamulani) ndiponso muvomereni Mtumiki Wake pamene akukuitanirani ku chimene chingakupatseni moyo (wabwino wa pa dziko lapansi ndi tsiku lachimaliziro). Ndipo dziwani kuti Allah amatchinga pakati pa munthu ndi mtima wake (amautembenula mmene akufunira). Ndipo dziwani kuti kwa Iye mudzasonkhanitsidwa.[195]
Ndipo muope mazunzo (a Allah a pano pa dziko lapansi) omwe sangagwere okhawo amene adzichitira zoipa mwa inu (koma adzawagweranso amene akusiya kuletsa zoipa) ndipo dziwani kuti Allah Ngolanga kwambiri.[196]
Ndipo kumbukirani (inu Asilamu) pamene mudali owerengeka, ochepa, onyozeka m’dziko. Mumakhala moopa anthu kuti angakufwambeni, koma anakupatsani pamalo pabwino pokhala, nakulimbikitsani ndi chipulumutso Chake, nakuninkhani zinthu zabwino kuti muyamike (Allah).[197]
E inu amene mwakhulupirira! Musachitire Allah ndi Mtumiki (Wake) chinyengo (pa kutsata zimene mwaletsedwa). Ndipo musazichitire chinyengo zimene mwakhulupirika nazo uku mukudziwa (kuti kutero ndikulakwa).
Ndipo dziwani kuti chuma chanu ndi ana anu ndimayesero (oyesedwa ndi Allah kuti aone mmene mungagwiritsire nazo ntchito). Ndi kuti kwa Allah kuli malipiro aakulu.
Ndipo (kumbukira) pamene omwe sadakhulupirire amakuchitira chiwembu kuti akunjate, kapena akuphe, kapena akutulutse (m’dziko lawo la Makka mwachipongwe). Ndipo amachita chiwembu, naye Allah anawononga chiwembu chawocho. Ndipo Allah ndiwokhoza koposa poononga ziwembu (za anthu oipa).[199]
Ndipo (kumbukira) pamene adati: “E Inu Allah! Ngati ichi (chimene wadza nacho Muhammad {s.a.w}) chili choonadi chochokera kwa Inu, tivumbwitsireni mvula ya miyala yochokera kumwamba, kapena mutibweretsere chilango chowawa kwambiri.”[200]
(Kodi iwo Aquraish) ali ndi chinthu chanji (chabwino chimene) chingamuletse Allah kuwalanga? Pomwe iwo akuwatsekereza anthu kulowa mu Msikiti Wopatulika. Iwo sanayenere kukhala ouyang’anira (Msikitiwo). Palibe angauyang’anire koma olungama, koma anthu ambiri sadziwa.[201]
Ndipo mapemphero awo pa nyumba yopatulikayo sadali kanthu, koma kuyimba miluzi ndi kuomba m’manja. Choncho (adzauzidwa): “Lawani chilango chifukwa chakusakhulupirira kwanu.”
Ndithu osakhulupirira akupereka chuma chawo (pa nkhondo yolimbana ndi Asilamu) ndi cholinga choti awatsekeleze anthu kuyenda pa njira ya Allah. Choncho adzapitiriza kupereka chumacho kenako chidzakhala chowadandaulitsa, ndipo adzagonjetsedwa. Ndipo omwe sanakhulupirire adzasonkhanitsidwa ku Jahannam.
Nena kwa osakhulupirira kuti: “Ngati asiya (zochita zawo zoipa), adzakhululukidwa zimene zidatsogola. Koma ngati abwereza (kuwazunza Asilamu, tiwalanga) ndithudi njira ya Allah yomwe idachitika kwa anthu akale inadutsa (powalanga akasiya kutsata malamulo a Allah).
۞ Ndipo dziwani kuti chilichonse chimene mwapeza monga chuma cholanda ku nkhondo, gawo limodzi mwa magawo asanu ndi cha Allah ndi Mtumiki, ndi a chibale (a Mtumiki), amasiye, masikini ndi munthu wa pa ulendo (amene asowedwa choyendera pa ulendo. Tsatilani malamulowa) ngatidi mwakhulupirira Allah ndi chimene tachivumbulutsa kwa kapolo Wathu pa tsiku lachilekanitso (lolekanitsa pakati pa choona ndi chabodza), tsiku limene magulu awiri adakumana (tsiku la nkhondo ya Badr, gulu la nkhondo la Asilamu ndi gulu la nkhondo la osakhulupirira). Ndipo Allah Ngokhoza kuchita chilichonse.
(Kumbukirani) pamene mudali mbali ya chigwa yoyandikira (mzinda wa Madina) pomwe iwo (ankhondo a Chikuraishi) adali mbali ya kutali ya tsidya lina (la chigwacho) pomwe aulendo amalonda adali cha kumunsi kwanu. Ngati mukadapangana nthawi yokumanirana (kuti mukumane nthawi yakutiyakuti), mukadasiyana posunga chipangano (chifukwa cha kuopa kuchuluka kwa adani anuwo). Koma (mwakumana mosayembekezera ndi ankhondo a adaniwo) kuti Allah akwaniritse chinthu chomwe nchofunika kuti chichitike, kuti awonongeke amene waonongeka (posankha kusakhulupirira) ndi umboni woonekera (umene adaukana kuutsata), ndi kuti akhale ndi moyo amene wakhala ndi moyo (amene watsata njira ya Chisilamu) ndi umboninso woonekera. Ndithudi Allah Ngwakumva zonse, Ngodziwa kwambiri.[202]
(Kumbukira) pamene Allah adakuonetsa iwo ku maloto kwako kuti ngochepa (pachiwerengero chawo potero udalimba mtima za kukumana nawo), akanakuonetsa iwo kuti ngambiri pa chiwerengero chawo; inu (Asilamu) mukadalephera (mukanataya mtima) ndipo mukanakangana pa chinthucho. (Ena akanafuna kumenyana nawo pamene ena akanakana), koma Allah anakutetezani (ku zimenezo). Ndithu Iye Ngodziwa kwambiri za m’mitima.
Ndipo (kumbukirani) pamene anakuonetsani iwo m’maso mwanu, pamene munakumana nawo kuti iwo ndi ochepa, (owerengeka, kuti mukhale ndi chidwi chomenyana nawo), ndiponso anakuchepetsani kwambiri m’maso mwawo (kuti iwo aone kuti nkosafunika kukonzekera kwambiri chifukwa chakuchepa kwa omenyana nawowo), kuti Allah akwaniritse chimene adalamula kuchitika. Kwa Allah Yekha ndiko kobwerera zinthu zonse.
Ndipo mumvereni Allah ndi Mtumiki Wake, musakangane (kuopera kuti) mungakhale olephera (ndi kutaya mtima), ndikuchoka mphamvu zanu. Koma pitirizani kupirira. Ndithudi, Allah ali pamodzi ndi anthu opirira.
Ndipo (kumbukira) pamene satana adawakometsera zochita zawo zoipa (aja osakhulupirira) nati: “Lero palibe aliyense mwa anthu amene angakugonjetseni, ndipo ine ndine mtetezi wanu.” Koma pamene magulu awiri ankhondo anaonana (anakumana pamaso ndi pamaso) satana anabwerera pambuyo (kuthawa) nati: “Ine ndikudzipatula mwa inu. Ndithu ine ndikuona zimene inu simukuziona. Ndithu ine ndikuopa Allah.” Ndipo Allah Ngwaukali polanga.
(Kumbukirani) pamene achiphamaso ndi amene ali ndi matenda m’mitima mwawo amanena: “Anthu awa chipembedzo chawo (cha Chisilamu) chawanyenga.” Komatu amene akuyadzamira kwa Allah ndithudi Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
Ndipo ukadaona angelo pamene akuchotsa miyoyo ya anthu amene sadakhulupirire (pa imfa yawo) uku akumenya kunkhope zawo ndi kumisana yawo (uku akunena): “Lawani chilango cha Moto woocha. (Ukadaziona zoopsa kwabasi).”
“Izo ndi chifukwa cha (machimo) amene manja anu anawatsogoza, ndipo Allah sali opondereza akapolo (Ake).”[203]
(Khalidwe lawo awa lili ) ngati khalidwe la anthu a Farawo ndi omwe adalipo patsogolo pawo. Anazikana zizindikiro za Allah, choncho Allah anawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndithudi Allah Ngwamphamvu, Wolanga moopsa.
Izo, (posawadzera miliri yotere) nchifukwa chakuti Allah sasintha chisomo (Chake) chimene wachipereka kwa anthu mpaka anthuwo asinthe okha zomwe zili m’mitima mwawo, (posiya kuthokoza Allah nayamba kuyenda m’njira zolakwira Allah). Ndithu Allah Ngwakumva Ngodziwa chilichonse.
Ndithu nyama zoipitsitsa kwa Allah ndi amene sakhulupirira. (amamkana Allah ngakhale choonadi akuchidziwa bwinobwino), choncho iwo sakhulupirira
Choncho, ngati uwapeza ku nkhondo, (menyana nawo), uwabalalitse (kuti likhale phunziro kwa) amene ali pambuyo pawo kuti iwo azindikire.
Ngati uopa kusakhulupirika kwa anthu (omwe unapangana nawo chipangano), atayire (chipangano chawocho), mwachilungamo; ndithu Allah sakonda (anthu) osakhulupirika.
Ndipo (anthu) amene sadakhulupirire asaganize kuti ampitilira (Allah kotero kuti sachita kanthu ndi iwo), iwo sangamulepheretse Allah (chimene akufuna kuchita pa iwo).
Ndipo ngati (awo adani) apendekera kumbali yokhalirana mwa mtendere, nawenso pendekera (ku mbaliyo) ukatero yadzamira kwa Allah. Ndithudi Iye Ngwakumva, Ngodziwa.
Ngati afuna kukunyenga pa chimvanochi, ndithudi, Allah akukwanira kwa iwe (kukuteteza). Iye ndi Yemwe anakuthangata ndi chipulumutso chake ndi okhulupirira.
Ndipo (Allah) analuzanitsa pakati pa mitima yawo (poika chikondi pakati pawo). Ngati ukanapereka zonse za m’dziko lapansi (ncholinga choti uwaluzanitse mitima yawo mwa iwe wekha) sukadatha kuluzanitsa pakati pa mitima yawo. Koma Allah adaluzanitsa pakati pawo. Ndithu Iye Ngwamphamvu zoposa Ngwanzeru zakuya.
E iwe Mneneri! Alimbikitse okhulupirira kupita ku nkhondo. Ngati mwa inu muli anthu makumi awiri olimba mtima (ndiye kuti) adzawagonjetsa mazana awiri (200) (a mwa anthu osakhulupirira). Ngati mwa inu muli anthu zana limodzi (100) (olimba mtima ndiye kuti) adzagonjetsa chikwi chimodzi (1,000) cha anthu omwe sadakhulupirire, chifukwa chakuti iwo ndi anthu osazindikira.
Sichoyenera kwa Mneneri kukhala ndi akayidi mpaka amenye nkhondo (kwambiri) ndi kugonjetseratu maiko molimba (ndi pamene atha kukhala ndi akayidi). Mukufuna zinthu za m’dziko pomwe Allah akufuna (mupeze mphoto ya) tsiku lachimaliziro! Ndipo Allah Ngwamphamvu zoposa Ngwanzeru zakuya.
Pakadapanda lamulo la Allah limene linatsogolera kale (lokulolezani chuma chopeza ku nkhondo), chilango chachikulu chikanakugwerani, chifukwa cha zimene munatenga (ku-nkhondo ya Badri).
Tsopano idyani chuma chimene mwalanda pa nkhondo (chomwe chili) chololedwa, chabwino, ndipo pitirizani kuopa Allah. Ndithu Allah Ngokhululuka, Ngwachisoni chosatha.
Ngati akufuna kukuchitirani chinyengo (chinyengo chawo sichiphula kanthu pa iwe), ndithu anamuchitirapo kale Allah chinyengo (chifukwa cha kusakhulupirira kwawo). Choncho anakupatsa mphamvu zowagonjetsera iwo. Ndipo Allah Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.
Ndithu anthu amene anakhulupirira nasamuka kwawo ndi kumenyana pa njira ya Allah ndi chuma chawo ndi moyo wawo; ndiponso amene anawalandira (iwo) ndi kuwapatsa malo ndi kuwathandiza, awa ndiabale otchinjirizana wina ndi mnzake. Ndipo anthu amene akhulupirira koma nasiya kusamuka (kudza ku Madina), palibe udindo pa inu wa kuwateteza kufikira nawonso atasamuka (kudza ku Madina). Ngati atakupemphani chithandizo cha chipembedzo athandizeni, kupatula (akaputana ndi anthu) amene pakati panu ndi iwo pali chipangano, (pamenepo musawathandize pomenyana ndi osakhulupirirawo omwe muli nawo chipangano). Ndipo Allah Ngowoona zomwe muchita.
Ndipo (anthu) amene sadakhulupirire (Allah) amatetezana okha ndi kukhala abwenzi pakati pawo. Ngati nanunso simuchita izi, padzakhala chisokonezo m’dziko ndi chionongeko chachikulu.
Amene akhulupirira nasamuka, namenya nkhondo panjira ya Allah (pamodzi nanu), ndiponso amene anawalandira (osamukawo), nawapatsa malo ndi kuwathandiza, iwo ndi omwe ali okhulupirira mwa choonadi. Iwo adzapeza chikhululuko ndi zopatsidwa za ulemu.
Ndipo aja akhulupirira pambuyo (pa Amuhajirina ndi Answari), nawonso nasamukira (ku Madina kukakhala pamodzi ndi Mtumiki ndi Asilamu anzawo), namenyanso nkhondo pamodzi nanu, iwo ndi amene ali mwa inu. Koma achibale chakubadwana, ndiamene ali oyenera (kulowerana mmalo pa chuma) ena ndi ena, mmene zilili) m’buku la Allah. Ndithudi, Allah Ngodziwa chilichonse.
Share