Surah Al-Anfal ( The Spoils of War ) - Aya 44
Surah Al-Anfal ( The Spoils of War ) - Chewa - Aya 44 Aya count 75
وَإِذْ يُرِيكُمُوهُمْ إِذِ ٱلْتَقَيْتُمْ فِىٓ أَعْيُنِكُمْ قَلِيلًۭا وَيُقَلِّلُكُمْ فِىٓ أَعْيُنِهِمْ لِيَقْضِىَ ٱللَّهُ أَمْرًۭا كَانَ مَفْعُولًۭا ۗ وَإِلَى ٱللَّهِ تُرْجَعُ ٱلْأُمُورُ ﴿٤٤﴾
Ndipo (kumbukirani) pamene anakuonetsani iwo m’maso mwanu, pamene munakumana nawo kuti iwo ndi ochepa, (owerengeka, kuti mukhale ndi chidwi chomenyana nawo), ndiponso anakuchepetsani kwambiri m’maso mwawo (kuti iwo aone kuti nkosafunika kukonzekera kwambiri chifukwa chakuchepa kwa omenyana nawowo), kuti Allah akwaniritse chimene adalamula kuchitika. Kwa Allah Yekha ndiko kobwerera zinthu zonse.