Surah Al-Anfal ( The Spoils of War ) - Aya 48

Surah Al-Anfal ( The Spoils of War ) - Chewa - Aya 48 Aya count 75

وَإِذْ زَيَّنَ لَهُمُ ٱلشَّيْطَٰنُ أَعْمَٰلَهُمْ وَقَالَ لَا غَالِبَ لَكُمُ ٱلْيَوْمَ مِنَ ٱلنَّاسِ وَإِنِّى جَارٌۭ لَّكُمْ ۖ فَلَمَّا تَرَآءَتِ ٱلْفِئَتَانِ نَكَصَ عَلَىٰ عَقِبَيْهِ وَقَالَ إِنِّى بَرِىٓءٌۭ مِّنكُمْ إِنِّىٓ أَرَىٰ مَا لَا تَرَوْنَ إِنِّىٓ أَخَافُ ٱللَّهَ ۚ وَٱللَّهُ شَدِيدُ ٱلْعِقَابِ ﴿٤٨﴾
Ndipo (kumbukira) pamene satana adawakometsera zochita zawo zoipa (aja osakhulupirira) nati: “Lero palibe aliyense mwa anthu amene angakugonjetseni, ndipo ine ndine mtetezi wanu.” Koma pamene magulu awiri ankhondo anaonana (anakumana pamaso ndi pamaso) satana anabwerera pambuyo (kuthawa) nati: “Ine ndikudzipatula mwa inu. Ndithu ine ndikuona zimene inu simukuziona. Ndithu ine ndikuopa Allah.” Ndipo Allah Ngwaukali polanga.
Share