Surah Al-Ma'un ( Small Kindnesses )

Surah Al-Ma'un ( Small Kindnesses ) - Chewa Aya count 7

Kodi wamuona yemwe akutsutsa za mphoto (ndi chiwerengero cha tsiku lachimaliziro)?[487]
Ndipo salimbikitsa (ena pamodzi ndi iye mwini) kudyetsa osauka.
Choncho kuonongeka kuli pa ena mwa opemphera swala (amene ali ndi mbiri izi);
Amenenso (akamachita mapemphero awo) amadzionetsera (kwa anthu mwachipha maso kuti apeze ulemelero ndi kutamandidwa mmitima mwa anthu).[489]
Ndipo amamana ziwiya (zawo posabwereka anzawo zinthu zofunika pa moyo wa aliyense monga nkhwangwa, mpeni, mtondo ndi zina zotere).
Share