Kodi wamuona yemwe akutsutsa za mphoto (ndi chiwerengero cha tsiku lachimaliziro)?[487]
Iye ndi yemwe akukankha wamasiye (mwankhanza).
Ndipo salimbikitsa (ena pamodzi ndi iye mwini) kudyetsa osauka.
Choncho kuonongeka kuli pa ena mwa opemphera swala (amene ali ndi mbiri izi);
Omwe amachitira mphwayi mapemphero awo.[488]
Amenenso (akamachita mapemphero awo) amadzionetsera (kwa anthu mwachipha maso kuti apeze ulemelero ndi kutamandidwa mmitima mwa anthu).[489]
Ndipo amamana ziwiya (zawo posabwereka anzawo zinthu zofunika pa moyo wa aliyense monga nkhwangwa, mpeni, mtondo ndi zina zotere).