Surah At-Taubah ( The Repentance ) - Aya 101

Surah At-Taubah ( The Repentance ) - Chewa - Aya 101 Aya count 129

وَمِمَّنْ حَوْلَكُم مِّنَ ٱلْأَعْرَابِ مُنَٰفِقُونَ ۖ وَمِنْ أَهْلِ ٱلْمَدِينَةِ ۖ مَرَدُوا۟ عَلَى ٱلنِّفَاقِ لَا تَعْلَمُهُمْ ۖ نَحْنُ نَعْلَمُهُمْ ۚ سَنُعَذِّبُهُم مَّرَّتَيْنِ ثُمَّ يُرَدُّونَ إِلَىٰ عَذَابٍ عَظِيمٍۢ ﴿١٠١﴾
Ndipo ena mwa Arabu a kuchimizi omwe akukhala m’mphepete mwanu (m’mphepete mwa mzinda wa Madina) alipo achiphamaso (achinyengo), ndiponso eni mzinda wa Madina aphunzira ukatswiri wachinyengo (kotero kuti) sukuwadziwa, Ife tikuwadziwa. Tiwalanga kawiri (pa dziko lapansi) ndipo kenako adzabwezedwa kuchilango chachikulu (pa tsiku lachimaliziro).
Share