Surah Al-Ma'arij (The Ways of Ascent )

Surah Al-Ma'arij (The Ways of Ascent ) - Chewa Aya count 44

Wopempha adapempha kuti chiwadzere msanga chilango chopezekacho, (m’kupempha kwa chipongwe ndi kotsutsa).
Choncho, pirira (iwe Mtumiki (s.a.w) kupirira kwabwino,
Ndithu iwo akuliona (tsiku la Qiyâma) kuti lili kutali (silingachitike).
Koma Ife tikuliona kuti lilipafupi (ndilochitika).
Tsiku limene thambo lidzakhala ngati mtovu wosungunuka.
Ndipo mapiri adzakhala ngati ubweya (wongouluka wokha).
Ngakhale adzawalole kuti aonane ndi kudziwana pakati pawo (sadzafunsana). Wochimwa adzalakalaka kuti akadaziwombola ku chilango cha tsiku limenelo ndi ana ake.
Iyayi, (siya iwe wamachimo zimene ukulakalakazo)! Ndithu umenewu ndi Moto wa malawi.
Udzaitana (potchula dzina la aliyense) amene adachitembenuzira msana choona ndi kunyoza.
Adasonkhanitsa (chuma) ndi kusunga (m’nkhokwe zake popanda kuperekera chopereka cha Allah).
Koma zabwino zikamkhudza amamana (ena ndi kuiwala mavuto amene adali nawo).
Kupatula opemphera Swala, (iwo alibe mbiri zoipazi).
Iwo amene sadukiza mapemphero awo a swala; (sakuwaleka ngakhale zivute chotani).
Ndi amene akuvomereza za tsiku la malipiro (ndi kumalikonzekera.)
Ndithu chilango cha Mbuye wawo nchosapulumuka nacho (munthu woipa).
Ndiponso iwo amene akusunga umaliseche wawo (posachita chiwerewere),
Amene ali ndi mbiri zimenezi adzakhala m’Minda (yamtendere) ali olemekezedwa.
Kodi kuli chiyani kwa amene akana (chikhulupiliro) akuthamangira kwa iwe (maso ali pamtunda)?
Asiye (kukhumba kwawo kokalowa ku Munda wamtendere)! Ndithu Ife tidawalenga kuchokera m’zimene akudziwa (madzi opanda pake).
Tsiku limene adzatuluke m’manda uku akuthamanga (kudza kwa woitana) ngati kuti akuthamangira kumafano awo (amene adali kuwapembedza).
Maso awo ali zyoli, (osatha kuwakweza); kuyaluka kutawaphimba! Limenelo ndilo tsiku lomwe adali kulonjezedwa (pomwe adali padziko lapansi.
Share