Surah At-Tahrim ( The Prohibition ) - Aya 4
Surah At-Tahrim ( The Prohibition ) - Chewa - Aya 4 Aya count 12
إِن تَتُوبَآ إِلَى ٱللَّهِ فَقَدْ صَغَتْ قُلُوبُكُمَا ۖ وَإِن تَظَٰهَرَا عَلَيْهِ فَإِنَّ ٱللَّهَ هُوَ مَوْلَىٰهُ وَجِبْرِيلُ وَصَٰلِحُ ٱلْمُؤْمِنِينَ ۖ وَٱلْمَلَٰٓئِكَةُ بَعْدَ ذَٰلِكَ ظَهِيرٌ ﴿٤﴾
Ngati awirinu mulapa kwa Allah pazimene mwachita (chitani changu kulapa) chifukwa chakuti mitima yanu yapotoka pang’ono (chifukwa cha nsanje pa zimene Mneneri akufuna zosunga chinsinsi Chake); koma ngati awirinu muthandizana pazimene zingamvutitse, ndithu Allah ndiye Mtetezi wake ndi Jibril (Gabriele) ndiponso okhulupirira abwino; naonso angelo, kuonjezera apa ndiathandizi (ake).