مَثَلُ ٱلَّذِينَ حُمِّلُوا۟ ٱلتَّوْرَىٰةَ ثُمَّ لَمْ يَحْمِلُوهَا كَمَثَلِ ٱلْحِمَارِ يَحْمِلُ أَسْفَارًۢا ۚ بِئْسَ مَثَلُ ٱلْقَوْمِ ٱلَّذِينَ كَذَّبُوا۟ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ ۚ وَٱللَّهُ لَا يَهْدِى ٱلْقَوْمَ ٱلظَّٰلِمِينَ ﴿٥﴾
Fanizo la (Ayuda) amene adawasenzetsa Taurat (pokakamizidwa kuti atsatire zophunzitsa za bukulo, koma osatsatira), ali ngati bulu amene akusenza mabuku akuluakulu anzeru, (koma osathandizika nawo). Taonani kuipa fanizo la anthu amene atsutsa zisonyezo za Allah. Ndipo Allah saongola anthu achinyengo.[362]