Zonse za kumwamba ndi za pansi zimalemekeza Allah (ndi kumuyeretsa ku khalidwe losayenera ndi ulemelero Wake). Ndipo Iye Ngopambana (salephera kanthu), Ngwaluntha (m’kakonzedwe Kake ndi m’zochita Zake).
Iye ndi Amene adatulutsa osakhulupirira ena mwa anthu a buku m’nyumba zawo mkusamusidwa koyamba (pa chilumba cha Arabu). Simunkaganizira kuti angatuluke (m’nyumba zawozo). Ndipo iwo amaganiza kuti malinga awo awateteza kwa Allah. Koma Allah adawalanga kupyolera mmene samayembekezera, ndipo adathira mantha oopsa m’mitima mwawo (potumiza Mtumiki Wake kwa iwo), adagumula nyumba zawo ndi manja awo ndi manja a okhulupirira. Choncho lingalirani (zimenezi) E inu eni nzeru! [353]
Ndipo kukadapanda kuti Allah adawalembera (pachiyambi) kusamuka (m’nyumba zawo), akadawalanga pa dziko pompano; koma chilango cha Moto chili pa iwo tsiku lachimaliziro.
Zimenezo nchifukwa chakuti iwo adamtsutsa Allah ndi Mthenga Wake, (kutsutsa kopyola muyeso); ndipo amene akutsutsa Allah (sangapulumuke ku chilango Chake). Ndithu Allah Ndiwolanga mwaukali.
Sim’dadule mtengo uliwonse wa zipatso za kanjedza, (inu Asilamu), kapena kuusiya uli chiimire ndi thunthu lake koma nchifuniro cha Allah ndi kuti awayalutse otuluka m’malamulo Ake.[354]
Ndipo chuma chimene wapereka Allah kwa Mtumiki Wake chochokera kwa iwo (Bani Nadhiri), chimenecho inu simudathamangitse mahachi kapena ngamira (pakuchipeza), koma Allah amapereka mphamvu kwa atumiki Ake zogonjetsera amene wamfuna. Ndipo Allah ali ndi Mphamvu (pa) chilichonse.
Chuma chimene Allah wachipereka kwa mtumiki Wake kuchokera kwa anthu am’midzi (yapafupi ndi mzinda wa Madina) chimenecho ncha Allah, ndi Mtumiki, ndi abale a mtumiki ndi amasiye, ndi masikini, ndiponso apaulendo; kuti chisakhale chongozungulira pakati pa olemera okha mwa inu. Ndipo chimene wakupatsani Mtumiki, chilandireni; ndipo chimene Wakuletsani chisiyeni. Muopeni Allah (potsatira malamulo Ake). Ndithu Allah Ngwaukali polanga.
(Chiperekedwe) kwa osauka osamuka omwe adatulutsidwa m’nyumba zawo ndi (kusiya) chuma chawo chifukwa chofuna zabwino za Allah ndi chikondi (Chake) ndi kupulumutsa (chipembedzo cha) Allah ndi Mthenga Wake (pogwiritsira ntchito matupi awo ndi chuma chawo); iwowa ndi (Asilamu) owona.
Koma amene adakhala kale mu mzinda uwu (wa Madina) ndi kukhulupirira akukonda amene adasamukira kwa iwo. Ndipo sakupeza vuto m’mitima mwawo pa zimene anzawo apatsidwa, ndipo akutsogoza zofuna za anzawo pa zawo, ngakhale iwo akuzifunitsitsa. Ndipo amene atetezedwa (ndi Allah) ku umbombo wa mitima yawo, amenewo ndiwo opambana.
Iye ndi Allah; Mlengi wa (zinthu, palibe chomfanizira); Muumbi wa chilichonse, Mkonzi wa maonekedwe a zinthu, Ake ndi maina abwino, zonse za kumwamba ndi pansi zikumulemekeza Iye ndi kumyeretsa ku makhalidwe osayenerana ndi ulemelero Wake. Iye Ngopambana ndiponso Wanzeru zakuya.