وَإِذْ قُلْتُمْ يَٰمُوسَىٰ لَن نَّصْبِرَ عَلَىٰ طَعَامٍۢ وَٰحِدٍۢ فَٱدْعُ لَنَا رَبَّكَ يُخْرِجْ لَنَا مِمَّا تُنۢبِتُ ٱلْأَرْضُ مِنۢ بَقْلِهَا وَقِثَّآئِهَا وَفُومِهَا وَعَدَسِهَا وَبَصَلِهَا ۖ قَالَ أَتَسْتَبْدِلُونَ ٱلَّذِى هُوَ أَدْنَىٰ بِٱلَّذِى هُوَ خَيْرٌ ۚ ٱهْبِطُوا۟ مِصْرًۭا فَإِنَّ لَكُم مَّا سَأَلْتُمْ ۗ وَضُرِبَتْ عَلَيْهِمُ ٱلذِّلَّةُ وَٱلْمَسْكَنَةُ وَبَآءُو بِغَضَبٍۢ مِّنَ ٱللَّهِ ۗ ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمْ كَانُوا۟ يَكْفُرُونَ بِـَٔايَٰتِ ٱللَّهِ وَيَقْتُلُونَ ٱلنَّبِيِّۦنَ بِغَيْرِ ٱلْحَقِّ ۗ ذَٰلِكَ بِمَا عَصَوا۟ وَّكَانُوا۟ يَعْتَدُونَ ﴿٦١﴾
Ndipo (kumbukiraninso nkhani iyi) pamene mudati: “E iwe Mûsa! Sitingathe kupirira ndi chakudya chamtundu umodzi (chomwe ndi Mana ndi Salwa); choncho tipemphere kwa Mbuye wako kuti atitulutsire (atipatse) ife zimene nthaka imameretsa, monga masamba, nkhaka, adyo, nyemba za mtundu wa chana ndi anyezi.” Iye adati: “Kodi mukufuna kusinthitsa chonyozeka ndi chabwino? Pitani m’midzi, ndipo kumeneko mukapeza zimene mwapemphazi.” Potero adapatsidwa kunyozeka ndi kusauka; nabwerera ndi mkwiyo wa Allah. Zimenezo n’chifukwa chakuti iwo sadali okhulupirira zisonyezo za Allah, ndikuti adali kupha aneneri a Allah popanda chifukwa. Zidali tero chifukwa cha kunyoza kwawo, ndipo adali olumpha malire.