وَقَالَ لَهُمْ نَبِيُّهُمْ إِنَّ ٱللَّهَ قَدْ بَعَثَ لَكُمْ طَالُوتَ مَلِكًۭا ۚ قَالُوٓا۟ أَنَّىٰ يَكُونُ لَهُ ٱلْمُلْكُ عَلَيْنَا وَنَحْنُ أَحَقُّ بِٱلْمُلْكِ مِنْهُ وَلَمْ يُؤْتَ سَعَةًۭ مِّنَ ٱلْمَالِ ۚ قَالَ إِنَّ ٱللَّهَ ٱصْطَفَىٰهُ عَلَيْكُمْ وَزَادَهُۥ بَسْطَةًۭ فِى ٱلْعِلْمِ وَٱلْجِسْمِ ۖ وَٱللَّهُ يُؤْتِى مُلْكَهُۥ مَن يَشَآءُ ۚ وَٱللَّهُ وَٰسِعٌ عَلِيمٌۭ ﴿٢٤٧﴾
Ndipo mneneri wawoyo adawauza: “Allah wakusankhirani Taluti kukhala mfumu. (Iwo ) adati: “Nchotani kuti iye akhale ndi ufumu pa ife pomwe ife ngoyenera kupeza ufumu kuposa iye, ndipo sadapatsidwe chuma chambiri?” (Iye) adati: “Ndithu Allah wamusankha pa inu, ndipo wamuonjezera kukhala ndi nzeru zopambana ndi kukhala ndi thupi (lamphamvu). Ndipo Allah amampatsa ufumu wake amene wamfuna. Ndipo Allah ndi Mwini zopereka zambiri, Ngodziwa.”