لِّلَّذِينَ يُؤْلُونَ مِن نِّسَآئِهِمْ تَرَبُّصُ أَرْبَعَةِ أَشْهُرٍۢ ۖ فَإِن فَآءُو فَإِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٌۭ رَّحِيمٌۭ ﴿٢٢٦﴾
Kwa omwe akulumbilira kuti adzipatula kwa akazi awo, (nyengo yawo) ayembekezere miyezi inayi. Koma ngati atabwerera (nakhala pamodzi ndi akazi awo), ndithudi Allah Ngokhululuka kwambiri, Ngwachisoni zedi. [34]