وَلِلَّهِ ٱلْمَشْرِقُ وَٱلْمَغْرِبُ ۚ فَأَيْنَمَا تُوَلُّوا۟ فَثَمَّ وَجْهُ ٱللَّهِ ۚ إِنَّ ٱللَّهَ وَٰسِعٌ عَلِيمٌۭ ﴿١١٥﴾
Ndipo kuvuma ndi kuzambwe nkwa Allah; ndipo pamalo paliponse pamene mwatembenukira, (pomwe Allah wakulamulirani kuti mutembenukire), pamenepo mupezapo chiyanjo cha Allah. Ndithudi Allah Ngokwanira ponseponse, Wodziwa chilichonse.