Ndikulumbilira mitengo ya Mkuyu ndi Zitona (pansi pa mitengo imeneyi Ibrahim ndi Nuh (Nowa) adapeza uneneri),
Ndi phiri la Sinai (pamene Allah adamulankhulira Mûsa),
Ndiponso mzinda uwu (wolemekezeka) wamtendere; (Makka, womwe adapatsiridwa uneneri Muhammad) (s.a.w).
Palibe chikaiko, tamulenga munthu mkalengedwe kabwino, kolingana (ndipo ali ndi mbiri zabwino).[457]
Pambuyo pake tamubwezera pansi kumposa wa pansi.[458]
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, adzakhala nawo iwo malipiro osatha.
Tsono nchiyani chakuchititsa kuti ukanire kuuka ndi malipiro pambuyo (poona mphamvu zathu pa chilichonse)?[459]
Kodi Allah si Muweruzi wa nzeru kuposa aweruzi onse?