Surah Al-Balad ( The City )

Surah Al-Balad ( The City ) - Chewa Aya count 20

Ndipo iwe udzatsikira mu mzindawu mwa ufulu (ndi kuuonjezera ulemelero).
Ndiponso ndikulumbilira chobereka ndi choberekedwa, (kudzera mwa iwo mtundu wa anthu udasungidwa).
Ndithudi tamulenga munthu mmavuto (kuyambira chiyambi chake mpaka malekezero a moyo wake).[439]
Kodi (munthu wolengedwa ndi mavutoyu) akuganiza kuti palibe amene angamuthe? [440]
Akunena (monyadira kuti): “Ndaononga chuma chambiri (chifukwa choletsa Chisilamu kufala).”[441]
Kodi sitidampangire maso awiri (amene akuyang’anira)?
Ndilirime ndi milomo iwiri (zimene akulankhulira)?
Ndipo tamlongosolera njira ziwiri: (yabwino ndi yoipa, ndipo tampatsa mphamvu yosankhira njira imene akufuna).
Kodi walikwera phiri lovutalo (lomwe lingakamfikitse ku Jannah)?[442]
Nanga nchiyani chakudziwitsa za kukwera phiri lovutalo?
(Kutero ndiko) kupereka ufulu kwa kapolo,
Kapena wosauka wa fumbi lokhalokha (chifukwa cha kuvutika kwambiri),
Moto wozungulira mbali zonse udzakhala pa iwo (ndikuwatsekera makomo).
Share