Surah Al-A'la ( The Most High )

Surah Al-A'la ( The Most High ) - Chewa Aya count 19

Lemekeza dzina la Mbuye wako Wapamwambamwamba (ndikuliyeretsa ku zinthu zosayenera).[417]
Amene adalenga (chilichonse) ndikuchikonza bwinobwino (mkalengedwe kolingana).
Amene adalamuliratu (chilichonse zochita zake) ndi kuchiongolera.[418]
Tikulakatulira (chivumbulutso Chathu) ndipo siuyiwala.[419]
Kupatula chimene wafuna Allah (kuti uchiiwale); ndithu Iye amadziwa zoonekera ndi zimene zimabisika.
Ndipo tikufewetsera (njira yochitira zinthu) zabwino.[420]
Choncho akumbutse (wanthu powalalikira) ngati kukumbutsa kuthandiza.[421]
(Palibe chikaiko ulalikiwo) aukumbukira (ndikuthandizidwa nawo) amene akuopa Allah.
Ndipo wamavuto ambiri, (wamakani ndi wokanira), adzitalikitsa ndi ulalikiwo.[422]
Amene adzalowa ku moto waukulu (umene wakonzedwa kuti udzakhale malipiro ake).
Ndipo sakafa m’menemo (ndikupumula kumazunzo), ndiponso sakakhala ndi moyo (wamtendere).
Ndithu wapambana amene wadziyeretsa (ku machimo),[423]
Ndikukumbukira dzina la Mbuye wake (ndi mtima wake, ndi lirime lake) uku akumapemphera.
Pamene moyo wa tsiku lachimaliziro ndiwabwino kwambiri ndiponso wamuyaya.
Ndithu izi (mukuuzidwa m’Qur’an) zilipo m’mabuku oyamba, akale,[424]
Share