Surah Al-Infitar ( The Cleaving )

Surah Al-Infitar ( The Cleaving ) - Chewa Aya count 19

Ndi pamene nyenyezi zidzayoyoke (ndi kumwazikana),
Pamenenso nyanja zikuluzikulu zidzaphwasulidwe.
Ndiponso pamene manda adzafukulidwe (ndikutuluka akufa omwe adali mmenemo),
(Panthawiyo) mzimu uliwonse udzadziwa zimene udatsogoza (zabwino ndi zoipa) ndi zimene udasiya m’mbuyo.[398]
E iwe munthu! Nchiani chakunyenga kumsiya Mbuye wako wa ufulu (kufikira pomnyoza)?
Amene adalenga iwe nakulinganiza (ziwalo zako) ndi kukulongosola (moyenera);
Ndipo maonekedwe amtundu uliwonse omwe adawafuna adakuveka (popanda chifuniro chako).
Ayi, sichoncho! Koma inu mukutsutsa za (tsiku) lamalipiro.
Olemekezeka, olemba (zochita zanu.)
Akudziwa (zonse) zimene mukuchita (zabwino ndi zoipa).
Ndipo ndithu amene ali olakwira malamulo a Allah adzakhala ku Moto wopsereza.
Limeneli ndi tsiku limene mzimu uliwonse sudzakhala ndi mphamvu (yodzetsa mtendere kapena yochotsa chovuta) pa mzimu wina. Ndipo lamulo pa tsiku limeneli ndi la Allah yekha.[400]
Share