Pamene dzuwa lidzakulungidwe (ndikuchotsedwa kuwala kwake),[388]
Ndi pamene nyenyezi zidzathothoke (ndi kuchoka dangalira lake),
Ndi pamene mapiri adzayendetsedwe (kuchoka mmalo mwake),[389]
Ndi pamene ngamira zabere lamiyezi khumi zidzasiidwe (zopanda oziyang’anira),[390]
Ndi pamene nyama za mtchire zidzasonkhanitsidwe pamodzi (kuchokera mmalo osiyanasiyana chifukwa chakuopsa kwakukulu kwa tsikulo),[391]
Ndi pamene nyanja zidzayatsidwe moto,
Ndi pamene mizimu idzalumikizidwe (ndi matupi ake),
Ndi pamene mwana wamkazi yemwe adaikidwa m’manda wamoyo adzafunsidwe,[392]
Ndi tchimo lanji adaphedwera?
Ndi pamene makalata (momwe mudalembedwa zochita za aliyense) adzatambasulidwe ndi kugawidwa (kuti awerengedwe),[393]
Ndi pamene thambo lidzayalulidwe (kuchoka mmalo mwake),
Ndi pamene Jahena idzasonkhezeredwe mwamphamvu,[394]
Ndi pamene Jannah idzayandikitsidwe,
(Zikadzachitika zimenezi) mzimu uliwonse udzadziwa zimene wabweretsa (zabwino ndi zoipa).
Ndikulumbilira nyenyezi zimene zimabwerera masana ndi kutulukanso usiku.
Zomwe zimayenda kenako nkubisika,
Ndi usiku pamene ukulowa.
Ndithu iyi (Qur’an) ndi liwu la mthenga wa Allah (Jibril) wolemekezeka,[395]
Mwini mphamvu ndi mwini ulemelero kwa Mwini Arsh (Mpando wa chifumu),
Womveredwa kumeneko ndiponso wokhulupirika (pachivumbulutso).
Ndipo m’bale wanuyu siwamisala ayi.[396]
Ndithu ndikulumbira kuti (iye Mtumiki) (s.a.w) adamuona (Jibril) mchizimezime (chakum’mawa) chooneka bwino.
Ndipo sali iye (Mtumiki) waumbombo ndi chivumbulutso (koma amafikitsa zonse ndi kuziphunzitsa kwa anthu).
(Chivumbulutso chomwe chavumbulutsidwachi kwa iye) si mawu a satana wothamangitsidwa (mchifundo cha Allah);
(Qur’ani) iyi sichina koma ndi chikumbutso cha zolengedwa zonse.
Kwa yemwe mwa inu akufuna kuyenda mu njira yoongoka.
Ndipo simungafune chinthu mwa inu nokha pokhapokha atafuna Allah Mbuye wa zolengedwa zonse.