يَعْمَلُونَ لَهُۥ مَا يَشَآءُ مِن مَّحَٰرِيبَ وَتَمَٰثِيلَ وَجِفَانٍۢ كَٱلْجَوَابِ وَقُدُورٍۢ رَّاسِيَٰتٍ ۚ ٱعْمَلُوٓا۟ ءَالَ دَاوُۥدَ شُكْرًۭا ۚ وَقَلِيلٌۭ مِّنْ عِبَادِىَ ٱلشَّكُورُ ﴿١٣﴾
Ziwandazi zimampangira zimene wafuna, monga: misikiti, zithunzi zokhala ndi matupi, ndi mabeseni onga madamu ndi midenga yokhazikika. (Tidawauza:) “Chitani ntchito zabwino, E inu akubanja la Daud! Pothokoza (madalitso amene mwapatsidwa). Komatu ndiochepa othokoza mwa akapolo Anga.”