قِيلَ لَهَا ٱدْخُلِى ٱلصَّرْحَ ۖ فَلَمَّا رَأَتْهُ حَسِبَتْهُ لُجَّةًۭ وَكَشَفَتْ عَن سَاقَيْهَا ۚ قَالَ إِنَّهُۥ صَرْحٌۭ مُّمَرَّدٌۭ مِّن قَوَارِيرَ ۗ قَالَتْ رَبِّ إِنِّى ظَلَمْتُ نَفْسِى وَأَسْلَمْتُ مَعَ سُلَيْمَٰنَ لِلَّهِ رَبِّ ٱلْعَٰلَمِينَ ﴿٤٤﴾
(Mfumukazi ija) idauzidwa kuti: “Lowa mkhonde la nyumba.” Koma pamene adaliona adaliganizira kuti ndidziwe; adakweza nsalu kumiyendo yake. (Sulaiman) adati: “Ndithu limeneli ndikhonde lomwe laziridwa ndi magalasi.” (Mfumukazi) idati: “E Mbuye wanga! Ndadzichitira ndekha chinyengo; choncho, ndagonjera kwa Allah, Mbuye wazolengedwa pamodzi ndi Sulaiman.”