Surah An-Naml (The Ants ) - Aya 40

Surah An-Naml (The Ants ) - Chewa - Aya 40 Aya count 93

قَالَ ٱلَّذِى عِندَهُۥ عِلْمٌۭ مِّنَ ٱلْكِتَٰبِ أَنَا۠ ءَاتِيكَ بِهِۦ قَبْلَ أَن يَرْتَدَّ إِلَيْكَ طَرْفُكَ ۚ فَلَمَّا رَءَاهُ مُسْتَقِرًّا عِندَهُۥ قَالَ هَٰذَا مِن فَضْلِ رَبِّى لِيَبْلُوَنِىٓ ءَأَشْكُرُ أَمْ أَكْفُرُ ۖ وَمَن شَكَرَ فَإِنَّمَا يَشْكُرُ لِنَفْسِهِۦ ۖ وَمَن كَفَرَ فَإِنَّ رَبِّى غَنِىٌّۭ كَرِيمٌۭ ﴿٤٠﴾
Yemwe adali ndi maphunziro (akuya) a m’buku adati: “Ine ndikubweletsera (chimpandocho) maso ako asadaphetire (usadatsinzine ndi kupenya).” Pamene adachiona chitakhazikitsidwa patsogolo pake, adati: “Izi nchifukwa cha ufulu wa Mbuye wanga kuti andiyese mayeso kodi ndithokoza kapena ndiusuliza (ufulu Wake). Ndipo amene akuthokoza ndithu ubwino wa kuthokozako udzakhala pa iye mwini. Ndipo amene akukana (mtendere wa Allah posathokoza), ndithu Mbuye wanga Ngokhupuka; Waulemu, (sasaukira chilichonse kwa anthu).”
Share