Surah Al-Masad ( The Palm Fibre )

Surah Al-Masad ( The Palm Fibre ) - Chewa Aya count 5

Aonongeka manja a Abi Lahab (omwe adali kuwagwiritsa ntchito pozunza Asilamu). Nayenso wawonongeka.[497]
Chuma chake ndi ulemelero wake (umene adaupeza) sizidamthandize ku chilango cha Allah.
Nayenso mkazi wake (adzalowa ku Moto) yemwe adali kusenza nkhuni (za minga pomutchera Mtumiki (s.a.w) komanso amanka nadanitsa pakati pa anthu).
Mkhosi mwake mdzamangidwa chingwe chopiringidwa bwino cha mlaza (chomlanga nacho).[498]
Share